< Masalimo 100 >

1 Salimo. Nyimbo yothokoza. Fuwulani kwa Yehova mwachimwemwe, inu dziko lonse lapansi.
A Psalm of praise. Make a joyful noise to the LORD, all ye lands.
2 Mulambireni Yehova mosangalala; bwerani pamaso pake ndi nyimbo zachikondwerero.
Serve the LORD with gladness: come before his presence with singing.
3 Dziwani kuti Yehova ndi Mulungu. Iye ndiye amene anatipanga ndipo ife ndife ake; ndife anthu ake, nkhosa za pabusa pake.
Know ye that the LORD he [is] God: [it is] he [that] hath made us, and not we ourselves; [we are] his people, and the sheep of his pasture.
4 Lowani ku zipata zake ndi chiyamiko ndi ku mabwalo ake ndi matamando; muyamikeni ndi kutamanda dzina lake.
Enter into his gates with thanksgiving, [and] into his courts with praise: be thankful to him, [and] bless his name.
5 Pakuti Yehova ndi wabwino ndipo chikondi chake ndi chamuyaya; kukhulupirika kwake nʼkokhazikika pa mibado ndi mibado.
For the LORD [is] good; his mercy [is] everlasting; and his truth [endureth] to all generations.

< Masalimo 100 >