< Masalimo 100 >
1 Salimo. Nyimbo yothokoza. Fuwulani kwa Yehova mwachimwemwe, inu dziko lonse lapansi.
“A psalm of praise.” Raise a voice of joy unto the LORD, all ye lands!
2 Mulambireni Yehova mosangalala; bwerani pamaso pake ndi nyimbo zachikondwerero.
Serve the LORD with gladness; Come before his presence with rejoicing!
3 Dziwani kuti Yehova ndi Mulungu. Iye ndiye amene anatipanga ndipo ife ndife ake; ndife anthu ake, nkhosa za pabusa pake.
Know ye that Jehovah is God! It is he that made us, and we are his, His people, and the flock of his pasture.
4 Lowani ku zipata zake ndi chiyamiko ndi ku mabwalo ake ndi matamando; muyamikeni ndi kutamanda dzina lake.
Enter into his gates with thanksgiving, And his courts with praise; Be thankful to him, and bless his name!
5 Pakuti Yehova ndi wabwino ndipo chikondi chake ndi chamuyaya; kukhulupirika kwake nʼkokhazikika pa mibado ndi mibado.
For the LORD is good; his mercy is everlasting; And his truth endureth to all generations.