< Masalimo 100 >
1 Salimo. Nyimbo yothokoza. Fuwulani kwa Yehova mwachimwemwe, inu dziko lonse lapansi.
A psalm of praise.
2 Mulambireni Yehova mosangalala; bwerani pamaso pake ndi nyimbo zachikondwerero.
Sing joyfully to God, all the earth: serve ye the Lord with gladness. Come in before his presence with exceeding great joy.
3 Dziwani kuti Yehova ndi Mulungu. Iye ndiye amene anatipanga ndipo ife ndife ake; ndife anthu ake, nkhosa za pabusa pake.
Know ye that the Lord he is God: he made us, and not we ourselves. We are his people and the sheep of his pasture.
4 Lowani ku zipata zake ndi chiyamiko ndi ku mabwalo ake ndi matamando; muyamikeni ndi kutamanda dzina lake.
Go ye into his gates with praise, into his courts with hymns: and give glory to him. Praise ye his name:
5 Pakuti Yehova ndi wabwino ndipo chikondi chake ndi chamuyaya; kukhulupirika kwake nʼkokhazikika pa mibado ndi mibado.
For the Lord is sweet, his mercy endureth for ever, and his truth to generation and generation.