< Masalimo 100 >

1 Salimo. Nyimbo yothokoza. Fuwulani kwa Yehova mwachimwemwe, inu dziko lonse lapansi.
Žalm k díků činění. Prokřikuj Hospodinu všecka země.
2 Mulambireni Yehova mosangalala; bwerani pamaso pake ndi nyimbo zachikondwerero.
Služte Hospodinu s veselím, předstupte před oblíčej jeho s prozpěvováním.
3 Dziwani kuti Yehova ndi Mulungu. Iye ndiye amene anatipanga ndipo ife ndife ake; ndife anthu ake, nkhosa za pabusa pake.
Vězte, že Hospodin jest Bůh; on učinil nás, a ne my sami sebe, abychom byli lid jeho, a ovce pastvy jeho.
4 Lowani ku zipata zake ndi chiyamiko ndi ku mabwalo ake ndi matamando; muyamikeni ndi kutamanda dzina lake.
Vcházejte do bran jeho s díkčiněním, a do síní jeho s chvalami; oslavujte jej, a dobrořečte jménu jeho.
5 Pakuti Yehova ndi wabwino ndipo chikondi chake ndi chamuyaya; kukhulupirika kwake nʼkokhazikika pa mibado ndi mibado.
Nebo dobrý jest Hospodin, na věky milosrdenství jeho, a od národu až do pronárodu pravda jeho.

< Masalimo 100 >