< Masalimo 10 >

1 Nʼchifukwa chiyani Yehova mwayima patali? Chifukwa chiyani mukudzibisa nokha pa nthawi ya mavuto?
Herre, hvi träder du så långt ifrå fördöljer dig i nödenes tid?
2 Mwa kunyada kwake munthu woyipa asaka wofowoka, amene akodwa mʼnjira zimene iye wakonza.
Så länge den ogudaktige öfverhandena hafver, måste den elände lida; de hålla med hvarannan, och upptänka arga list.
3 Iye amatamandira zokhumba za mu mtima wake; amadalitsa aumbombo ndi kuchitira chipongwe Yehova.
Ty den ogudaktige berömmer sig af sitt sjelfsvåld; och den giruge välsignar sig, och lastar Herran.
4 Mwa kunyada kwake woyipa safunafuna Mulungu; mʼmaganizo ake wonse mulibe malo a Mulungu.
Den ogudaktige är så stolt och vred, att han frågar efter ingen; uti alla sina tankar håller han Gud för intet.
5 Zinthu zake zimamuyendera bwino; iye ndi wamwano ndipo malamulo anu ali nawo kutali; amanyogodola adani ake onse.
Han håller fram med det han förehafver; dine domar äro fjerran ifrå honom; han handlar högmodeliga med alla sina fiendar.
6 Iye amadziyankhulira kuti, “Palibe chimene chidzandigwedeze. Ndidzakhala wokondwa nthawi zonse ndipo sindidzakhala pa mavuto.”
Han säger i sitt hjerta: Jag varder aldrig omstött; det skall ingen nöd hafva i evig tid.
7 Mʼkamwa mwake mwadzaza matemberero, mabodza ndi zoopseza; zovutitsa ndi zoyipa zili pansi pa lilime lake.
Hans mun är full med bannor, falskhet och bedrägeri; hans tunga kommer mödo och arbete åstad.
8 Iye amabisalira anthu pafupi ndi midzi, kuchokera pobisalapo amapha anthu osalakwa, amayangʼanayangʼana mwachinsinsi anthu oti awawononge.
Han sitter i försåt i gårdomen; han dräper de oskyldiga hemliga; hans ögon vakta efter de fattiga.
9 Amabisalira anthu ngati mkango pa zitsamba. Amabisalira kuti agwire anthu opanda mphamvu; amagwira anthu opanda mphamvu ndi kuwakokera mu ukonde wake.
Han vaktar i hemlig rum, såsom ett lejon i kulone; han vaktar efter, att han må gripa den elända; och han griper honom, då han drager honom i sitt nät.
10 Anthuwo amawapondaponda ndipo amakomoka; amakhala pansi pa mphamvu zake.
Han förkrossar och nedertrycker, och till jordena slår den fattiga med våld.
11 Iye amati mu mtima mwake, “Mulungu wayiwala, wabisa nkhope yake ndipo sakuonanso.”
Han säger i sitt hjerta: Gud hafver förgätit det; han hafver bortdolt sitt ansigte, han ser det aldrig.
12 Dzukani Yehova! Onetsani dzanja lanu Inu Mulungu. Musayiwale anthu opanda mphamvu.
Statt upp, Herre Gud; upphäf dina hand; förgät icke den elända.
13 Nʼchifukwa chiyani munthu woyipa amachitira chipongwe Mulungu? Chifukwa chiyani amati mu mtima mwake, “Iye sandiyimba mlandu?”
Hvi skall den ogudaktige försmäda Gud, och i sitt hjerta säga: Du sköter der intet om?
14 Komatu Inu Mulungu, mumazindikira mavuto ndi zosautsa, mumaganizira zochitapo kanthu. Wovutikayo amadzipereka yekha kwa Inu pakuti Inu ndi mthandizi wa ana amasiye.
Du ser det ju; förty du skådar vedermödo och jämmer, det står i dina händer; de fattige befalla det dig; du äst de faderlösas hjelpare.
15 Thyolani dzanja la woyipitsitsa ndi la munthu woyipa; muzengeni mlandu chifukwa cha zoyipa zake zimene sizikanadziwika.
Bryt sönder dens ogudaktigas arm, och besök det onda; så skall man hans ogudaktiga väsende intet mer finna.
16 Yehova ndi Mfumu kwamuyaya; mitundu ya anthu idzawonongeka kuchoka mʼdziko lake.
Herren är Konung alltid och evinnerliga; Hedningarna måste förgås utu hans land.
17 Mumamva Inu Yehova, zokhumba za osautsidwa; mumawalimbikitsa ndipo mumamva kulira kwawo.
De fattigas trängtan hörer du, Herre; deras hjerta är visst, att ditt öra aktar deruppå;
18 Kuteteza ana amasiye ndi oponderezedwa, ndi cholinga chakuti munthu amene ali wa dziko lapansi asaopsenso.
Att du skaffar dem faderlösa och fattiga rätt; att menniskan icke mer skall högmodas på jordene.

< Masalimo 10 >