< Masalimo 10 >

1 Nʼchifukwa chiyani Yehova mwayima patali? Chifukwa chiyani mukudzibisa nokha pa nthawi ya mavuto?
Пентру че стай аша де департе, Доамне? Пентру че Те аскунзь ла време де неказ?
2 Mwa kunyada kwake munthu woyipa asaka wofowoka, amene akodwa mʼnjira zimene iye wakonza.
Чел рэу, ын мындрия луй, урмэреште пе чей ненорочиць ши ей кад жертфэ курселор урзите де ел.
3 Iye amatamandira zokhumba za mu mtima wake; amadalitsa aumbombo ndi kuchitira chipongwe Yehova.
Кэч чел рэу се фэлеште ку пофта луй, яр рэпиторул батжокореште ши несокотеште пе Домнул.
4 Mwa kunyada kwake woyipa safunafuna Mulungu; mʼmaganizo ake wonse mulibe malo a Mulungu.
Чел рэу зиче ку труфие: „Ну педепсеште Домнул! Ну есте Думнезеу!” Ятэ тоате гындуриле луй.
5 Zinthu zake zimamuyendera bwino; iye ndi wamwano ndipo malamulo anu ali nawo kutali; amanyogodola adani ake onse.
Требуриле ый мерг бине ын орьче време; жудекэциле Тале сунт пря ыналте пентру ел, ка сэ ле поатэ ведя, ши суфлэ ку диспрец ымпотрива тутурор потривничилор луй.
6 Iye amadziyankhulira kuti, “Palibe chimene chidzandigwedeze. Ndidzakhala wokondwa nthawi zonse ndipo sindidzakhala pa mavuto.”
Ел зиче ын инима луй: „Ну мэ клатин, ын вечь сунт скутит де ненорочире!”
7 Mʼkamwa mwake mwadzaza matemberero, mabodza ndi zoopseza; zovutitsa ndi zoyipa zili pansi pa lilime lake.
Гура ый есте плинэ де блестеме, де ыншелэторий ши де виклешугурь ши суб лимбэ аре рэутате ши фэрэделеӂе.
8 Iye amabisalira anthu pafupi ndi midzi, kuchokera pobisalapo amapha anthu osalakwa, amayangʼanayangʼana mwachinsinsi anthu oti awawononge.
Стэ ла пындэ лынгэ сате ши учиде пе чел невиноват ын локурь досниче; окий луй пындеск пе чел ненорочит.
9 Amabisalira anthu ngati mkango pa zitsamba. Amabisalira kuti agwire anthu opanda mphamvu; amagwira anthu opanda mphamvu ndi kuwakokera mu ukonde wake.
Стэ ла пындэ ын аскунзэтоаря луй, ка леул ын визуинэ: стэ ла пындэ сэ приндэ пе чел ненорочит. Ыл принде ши-л траӂе ын лацул луй;
10 Anthuwo amawapondaponda ndipo amakomoka; amakhala pansi pa mphamvu zake.
се ындоае, се плякэ ши-й кад сэрачий ын гяре!
11 Iye amati mu mtima mwake, “Mulungu wayiwala, wabisa nkhope yake ndipo sakuonanso.”
Ел зиче ын инима луй: „Думнезеу уйтэ! Ышь аскунде Фаца ши ын вяк ну ва ведя!”
12 Dzukani Yehova! Onetsani dzanja lanu Inu Mulungu. Musayiwale anthu opanda mphamvu.
Скоалэ-Те, Доамне Думнезеуле, ридикэ мына! Ну уйта пе чей ненорочиць!
13 Nʼchifukwa chiyani munthu woyipa amachitira chipongwe Mulungu? Chifukwa chiyani amati mu mtima mwake, “Iye sandiyimba mlandu?”
Пентру че сэ хуляскэ чел рэу пе Думнезеу? Пентру че сэ зикэ ын инима луй кэ Ту ну педепсешть?
14 Komatu Inu Mulungu, mumazindikira mavuto ndi zosautsa, mumaganizira zochitapo kanthu. Wovutikayo amadzipereka yekha kwa Inu pakuti Inu ndi mthandizi wa ana amasiye.
Дар Ту везь; кэч Ту привешть неказул ши суферинца, ка сэ ей ын мынэ причина лор. Ын нэдеждя Та се ласэ чел ненорочит ши Ту вий ын ажутор орфанулуй.
15 Thyolani dzanja la woyipitsitsa ndi la munthu woyipa; muzengeni mlandu chifukwa cha zoyipa zake zimene sizikanadziwika.
Здробеште брацул челуй рэу, педепсеште-й фэрэделеӂиле, ка сэ пярэ дин окий Тэй!
16 Yehova ndi Mfumu kwamuyaya; mitundu ya anthu idzawonongeka kuchoka mʼdziko lake.
Домнул есте Ымпэрат ын вечь де вечь; нямуриле сунт нимичите дин цара Луй.
17 Mumamva Inu Yehova, zokhumba za osautsidwa; mumawalimbikitsa ndipo mumamva kulira kwawo.
Ту аузь ругэчуниле челор че суферэ, Доамне! Ле ынтэрешть инима, Ыць плечь урекя спре ей,
18 Kuteteza ana amasiye ndi oponderezedwa, ndi cholinga chakuti munthu amene ali wa dziko lapansi asaopsenso.
ка сэ фачь дрептате орфанулуй ши челуй асуприт ши ка сэ ну май инсуфле гроаза омул чел луат дин пэмынт.

< Masalimo 10 >