< Masalimo 10 >
1 Nʼchifukwa chiyani Yehova mwayima patali? Chifukwa chiyani mukudzibisa nokha pa nthawi ya mavuto?
Panie! przeczże stoisz z daleka? przeczże się ukrywasz czasu ucisku?
2 Mwa kunyada kwake munthu woyipa asaka wofowoka, amene akodwa mʼnjira zimene iye wakonza.
Złośnik z hardości prześladuje ubogiego; niechajże będą uchwyceni w chytrych zamysłach, które zamyślają.
3 Iye amatamandira zokhumba za mu mtima wake; amadalitsa aumbombo ndi kuchitira chipongwe Yehova.
Bo się chlubi niezbożnik w pożądliwościach duszy swojej, a łakomy błogosławi sobie a draźni Pana.
4 Mwa kunyada kwake woyipa safunafuna Mulungu; mʼmaganizo ake wonse mulibe malo a Mulungu.
Niepobożny dla pychy, którą po sobie pokazuje, nie pyta się o Boga; wszystka myśl jego, że niemasz Boga.
5 Zinthu zake zimamuyendera bwino; iye ndi wamwano ndipo malamulo anu ali nawo kutali; amanyogodola adani ake onse.
Darzą mu się drogi jego na każdy czas; dalekie są sądy twoje od niego; sapa przeciwko wszystkim nieprzyjaciołom swym.
6 Iye amadziyankhulira kuti, “Palibe chimene chidzandigwedeze. Ndidzakhala wokondwa nthawi zonse ndipo sindidzakhala pa mavuto.”
Mówi w sercu swem: Nie będę wzruszony od narodu do narodu; bo się nie boję złego.
7 Mʼkamwa mwake mwadzaza matemberero, mabodza ndi zoopseza; zovutitsa ndi zoyipa zili pansi pa lilime lake.
Usta jego pełne są złorzeczeństwa, i chytrości, i zdrady; pod językiem jego uprzykrzenie i nieprawość.
8 Iye amabisalira anthu pafupi ndi midzi, kuchokera pobisalapo amapha anthu osalakwa, amayangʼanayangʼana mwachinsinsi anthu oti awawononge.
Siedzi, czyhając we wsiach, w skrytościach zabija niewinnego; oczy jego upatrują ubogiego.
9 Amabisalira anthu ngati mkango pa zitsamba. Amabisalira kuti agwire anthu opanda mphamvu; amagwira anthu opanda mphamvu ndi kuwakokera mu ukonde wake.
Czyha w skrytem miejscu, jako lew w jamie swojej; dybie jakoby uchwycił ubogiego, ułapiwszy go ciągnie do sieci swojej.
10 Anthuwo amawapondaponda ndipo amakomoka; amakhala pansi pa mphamvu zake.
Przypada, przytula się, i rzuca się mocą swoją na wiele ubogich.
11 Iye amati mu mtima mwake, “Mulungu wayiwala, wabisa nkhope yake ndipo sakuonanso.”
Mówi w sercu swem: Zapomnałci tego Bóg; zakrył oblicze swoje, nie ujrzy na wieki.
12 Dzukani Yehova! Onetsani dzanja lanu Inu Mulungu. Musayiwale anthu opanda mphamvu.
Powstańże, Panie Boże! podnieś rękę twoję; nie zapominajże ubogich.
13 Nʼchifukwa chiyani munthu woyipa amachitira chipongwe Mulungu? Chifukwa chiyani amati mu mtima mwake, “Iye sandiyimba mlandu?”
Przeczże niezbożnik draźni Boga, mówiąc w sercu swem: Nie będziesz się o tem pytał?
14 Komatu Inu Mulungu, mumazindikira mavuto ndi zosautsa, mumaganizira zochitapo kanthu. Wovutikayo amadzipereka yekha kwa Inu pakuti Inu ndi mthandizi wa ana amasiye.
Ale ty widzisz ucisk, i krzywdę upatrujesz, abyś im odpłacił ręką twą; na ciebieć się spuścił ubogi, tyś jest pomocnikiem sierocie.
15 Thyolani dzanja la woyipitsitsa ndi la munthu woyipa; muzengeni mlandu chifukwa cha zoyipa zake zimene sizikanadziwika.
Potrzyj ramię niepobożnego i złośnika, dowiaduj się o jego niezbożności, aż go nie stanie.
16 Yehova ndi Mfumu kwamuyaya; mitundu ya anthu idzawonongeka kuchoka mʼdziko lake.
Pan jest królem na wieki wieczne; ale narody zginą z ziemi jego.
17 Mumamva Inu Yehova, zokhumba za osautsidwa; mumawalimbikitsa ndipo mumamva kulira kwawo.
Żądości pokornych wysłuchiwasz, Panie! utwierdzasz serca ich, nachylasz ku nim ucha twojego.
18 Kuteteza ana amasiye ndi oponderezedwa, ndi cholinga chakuti munthu amene ali wa dziko lapansi asaopsenso.
Abyś sąd uczynił sierocie i chudzinie, aby go więcej nie trapił człowiek śmiertelny na ziemi.