< Masalimo 10 >
1 Nʼchifukwa chiyani Yehova mwayima patali? Chifukwa chiyani mukudzibisa nokha pa nthawi ya mavuto?
. Pourquoi, Seigneur, vous êtes-vous retiré au loin, et avez-vous détourné de moi vos regards au temps du besoin, dans la tribulation?
2 Mwa kunyada kwake munthu woyipa asaka wofowoka, amene akodwa mʼnjira zimene iye wakonza.
. Pendant que l’impie s’enorgueillit, le pauvre est persécuté avec ardeur; ils sont pris dans les projets qu’ils forment.
3 Iye amatamandira zokhumba za mu mtima wake; amadalitsa aumbombo ndi kuchitira chipongwe Yehova.
. Parce que le pécheur est loué dans les désirs de son âme, et que le méchant est béni.
4 Mwa kunyada kwake woyipa safunafuna Mulungu; mʼmaganizo ake wonse mulibe malo a Mulungu.
. Le pécheur a irrité le Seigneur; il ne se mettra pas en peine de la grandeur de sa colère.
5 Zinthu zake zimamuyendera bwino; iye ndi wamwano ndipo malamulo anu ali nawo kutali; amanyogodola adani ake onse.
. Dieu n’est point devant ses yeux; ses voies sont souillées en tout temps. Vos jugements sont ôtés de devant sa vue; il dominera tous ses ennemis.
6 Iye amadziyankhulira kuti, “Palibe chimene chidzandigwedeze. Ndidzakhala wokondwa nthawi zonse ndipo sindidzakhala pa mavuto.”
. Car il a dit dans son cœur: Je ne serai point ébranlé; de génération en génération je serai sans aucun mal.
7 Mʼkamwa mwake mwadzaza matemberero, mabodza ndi zoopseza; zovutitsa ndi zoyipa zili pansi pa lilime lake.
. Sa bouche est pleine de malédiction, d’amertume et de fraude: sous sa langue sont le travail et la douleur.
8 Iye amabisalira anthu pafupi ndi midzi, kuchokera pobisalapo amapha anthu osalakwa, amayangʼanayangʼana mwachinsinsi anthu oti awawononge.
. Il est assis en embuscade avec les riches, dans des lieux cachés, afin de tuer l’innocent.
9 Amabisalira anthu ngati mkango pa zitsamba. Amabisalira kuti agwire anthu opanda mphamvu; amagwira anthu opanda mphamvu ndi kuwakokera mu ukonde wake.
. Ses yeux observent le pauvre: il lui dresse des embûches dans le secret, comme un lion dans sa caverne. Il dresse des embûches pour prendre le pauvre; pour prendre le pauvre, tandis qu’il l’attire.
10 Anthuwo amawapondaponda ndipo amakomoka; amakhala pansi pa mphamvu zake.
. Quand il l’aura dans son filet, il le renversera, il s’inclinera, et tombera, lorsqu’il se sera rendu maître des pauvres.
11 Iye amati mu mtima mwake, “Mulungu wayiwala, wabisa nkhope yake ndipo sakuonanso.”
. Car il a dit dans son cœur: Dieu a perdu le souvenir, il a détourné sa face pour ne rien voir à jamais.
12 Dzukani Yehova! Onetsani dzanja lanu Inu Mulungu. Musayiwale anthu opanda mphamvu.
. Levez-vous, Seigneur Dieu, que votre main s’élève: n’oubliez pas les pauvres.
13 Nʼchifukwa chiyani munthu woyipa amachitira chipongwe Mulungu? Chifukwa chiyani amati mu mtima mwake, “Iye sandiyimba mlandu?”
. Pourquoi l’impie a-t-il irrité Dieu? C’est qu’il a dit dans son cœur: Il n’en recherchera pas la vengeance.
14 Komatu Inu Mulungu, mumazindikira mavuto ndi zosautsa, mumaganizira zochitapo kanthu. Wovutikayo amadzipereka yekha kwa Inu pakuti Inu ndi mthandizi wa ana amasiye.
. Vous le voyez; car vous considérez le travail et la douleur, afin de livrer les oppresseurs entre vos mains. Le pauvre vous est abandonné; c’est vous qui serez le protecteur de l’orphelin.
15 Thyolani dzanja la woyipitsitsa ndi la munthu woyipa; muzengeni mlandu chifukwa cha zoyipa zake zimene sizikanadziwika.
. Brisez le bras du pécheur et du méchant; l’on cherchera son péché, et on ne le trouvera pas.
16 Yehova ndi Mfumu kwamuyaya; mitundu ya anthu idzawonongeka kuchoka mʼdziko lake.
. Le Seigneur régnera éternellement et dans les siècles des siècles: nations, vous serez exterminées de la terre.
17 Mumamva Inu Yehova, zokhumba za osautsidwa; mumawalimbikitsa ndipo mumamva kulira kwawo.
. Le Seigneur a exaucé le désir des pauvres: votre oreille a entendu la préparation de leur cœur:
18 Kuteteza ana amasiye ndi oponderezedwa, ndi cholinga chakuti munthu amene ali wa dziko lapansi asaopsenso.
. Afin de rendre justice à l’orphelin et au faible, afin que l’homme cesse de s’élever d’orgueil sur la terre.