< Masalimo 10 >
1 Nʼchifukwa chiyani Yehova mwayima patali? Chifukwa chiyani mukudzibisa nokha pa nthawi ya mavuto?
Pourquoi, Yahweh, te tiens-tu éloigné? et te caches-tu au temps de la détresse?
2 Mwa kunyada kwake munthu woyipa asaka wofowoka, amene akodwa mʼnjira zimene iye wakonza.
Quand le méchant s’enorgueillit, les malheureux sont consumés; ils sont pris dans les intrigues qu’il a conçues.
3 Iye amatamandira zokhumba za mu mtima wake; amadalitsa aumbombo ndi kuchitira chipongwe Yehova.
Car le méchant se glorifie de sa convoitise; le ravisseur maudit, méprise Yahweh.
4 Mwa kunyada kwake woyipa safunafuna Mulungu; mʼmaganizo ake wonse mulibe malo a Mulungu.
Dans son arrogance, le méchant dit: « Il ne punit pas! » « Il n’y a pas de Dieu «: voilà toutes ses pensées.
5 Zinthu zake zimamuyendera bwino; iye ndi wamwano ndipo malamulo anu ali nawo kutali; amanyogodola adani ake onse.
Ses voies sont prospères en tout temps! Tes jugements sont trop élevés pour qu’il s’en inquiète; tous ses adversaires, il les dissipe d’un souffle.
6 Iye amadziyankhulira kuti, “Palibe chimene chidzandigwedeze. Ndidzakhala wokondwa nthawi zonse ndipo sindidzakhala pa mavuto.”
Il dit dans son cœur: « Je ne serai pas ébranlé, je suis pour toujours à l’abri du malheur. »
7 Mʼkamwa mwake mwadzaza matemberero, mabodza ndi zoopseza; zovutitsa ndi zoyipa zili pansi pa lilime lake.
Sa bouche est pleine de malédiction, de tromperie et de violence; sous sa langue est la malice et l’iniquité.
8 Iye amabisalira anthu pafupi ndi midzi, kuchokera pobisalapo amapha anthu osalakwa, amayangʼanayangʼana mwachinsinsi anthu oti awawononge.
Il se met en embuscade près des hameaux, dans les lieux couverts il assassine l’innocent. Ses yeux épient l’homme sans défense,
9 Amabisalira anthu ngati mkango pa zitsamba. Amabisalira kuti agwire anthu opanda mphamvu; amagwira anthu opanda mphamvu ndi kuwakokera mu ukonde wake.
il est aux aguets dans le lieu couvert, comme un lion dans son fourré; il est aux aguets pour surprendre le pauvre, il se saisit du pauvre en le tirant dans son filet.
10 Anthuwo amawapondaponda ndipo amakomoka; amakhala pansi pa mphamvu zake.
Il se courbe, il se baisse, et les malheureux tombent dans ses griffes.
11 Iye amati mu mtima mwake, “Mulungu wayiwala, wabisa nkhope yake ndipo sakuonanso.”
Il dit dans son cœur: « Dieu a oublié! Il a couvert sa face, il ne voit jamais rien. »
12 Dzukani Yehova! Onetsani dzanja lanu Inu Mulungu. Musayiwale anthu opanda mphamvu.
Lève-toi, Yahweh; ô Dieu, lève ta main! N’oublie pas les affligés.
13 Nʼchifukwa chiyani munthu woyipa amachitira chipongwe Mulungu? Chifukwa chiyani amati mu mtima mwake, “Iye sandiyimba mlandu?”
Pourquoi le méchant méprise-t-il Dieu? Pourquoi dit-il en son cœur: « Tu ne punis pas? »
14 Komatu Inu Mulungu, mumazindikira mavuto ndi zosautsa, mumaganizira zochitapo kanthu. Wovutikayo amadzipereka yekha kwa Inu pakuti Inu ndi mthandizi wa ana amasiye.
Tu as vu pourtant; car tu regardes la peine et la souffrance, pour prendre en main leur cause. A toi s’abandonne le malheureux, à l’orphelin tu viens en aide.
15 Thyolani dzanja la woyipitsitsa ndi la munthu woyipa; muzengeni mlandu chifukwa cha zoyipa zake zimene sizikanadziwika.
Brise le bras du méchant; l’impie, — si tu cherches son crime, ne le trouveras-tu pas?
16 Yehova ndi Mfumu kwamuyaya; mitundu ya anthu idzawonongeka kuchoka mʼdziko lake.
Yahweh est roi à jamais et pour l’éternité, les nations seront exterminées de sa terre.
17 Mumamva Inu Yehova, zokhumba za osautsidwa; mumawalimbikitsa ndipo mumamva kulira kwawo.
Tu as entendu le désir des affligés, Yahweh; tu affermis leur cœur, tu prêtes une oreille attentive,
18 Kuteteza ana amasiye ndi oponderezedwa, ndi cholinga chakuti munthu amene ali wa dziko lapansi asaopsenso.
pour rendre justice à l’orphelin et à l’opprimé, afin que l’homme, tiré de la terre, cesse d’inspirer l’effroi.