< Masalimo 10 >

1 Nʼchifukwa chiyani Yehova mwayima patali? Chifukwa chiyani mukudzibisa nokha pa nthawi ya mavuto?
Lord, whi hast thou go fer awei? thou dispisist `in couenable tymes in tribulacioun.
2 Mwa kunyada kwake munthu woyipa asaka wofowoka, amene akodwa mʼnjira zimene iye wakonza.
While the wickid is proud, the pore man is brent; thei ben taken in the counsels, bi whiche thei thenken.
3 Iye amatamandira zokhumba za mu mtima wake; amadalitsa aumbombo ndi kuchitira chipongwe Yehova.
Forwhi the synnere is preisid in the desiris of his soule; and the wickid is blessid.
4 Mwa kunyada kwake woyipa safunafuna Mulungu; mʼmaganizo ake wonse mulibe malo a Mulungu.
The synnere `wraththide the Lord; vp the multitude of his ire he schal not seke.
5 Zinthu zake zimamuyendera bwino; iye ndi wamwano ndipo malamulo anu ali nawo kutali; amanyogodola adani ake onse.
God is not in his siyt; hise weies ben defoulid in al tyme. God, thi domes ben takun awei fro his face; he schal be lord of alle hise enemyes.
6 Iye amadziyankhulira kuti, “Palibe chimene chidzandigwedeze. Ndidzakhala wokondwa nthawi zonse ndipo sindidzakhala pa mavuto.”
For he seide in his herte, Y schal not be moued, fro generacioun in to generacioun without yuel.
7 Mʼkamwa mwake mwadzaza matemberero, mabodza ndi zoopseza; zovutitsa ndi zoyipa zili pansi pa lilime lake.
`Whos mouth is ful of cursyng, and of bitternesse, and of gyle; trauel and sorewe is vndur his tunge.
8 Iye amabisalira anthu pafupi ndi midzi, kuchokera pobisalapo amapha anthu osalakwa, amayangʼanayangʼana mwachinsinsi anthu oti awawononge.
He sittith in aspies with ryche men in priuytees; to sle the innocent man.
9 Amabisalira anthu ngati mkango pa zitsamba. Amabisalira kuti agwire anthu opanda mphamvu; amagwira anthu opanda mphamvu ndi kuwakokera mu ukonde wake.
Hise iyen biholden on a pore man; he settith aspies in hid place, as a lioun in his denne. He settith aspies, for to rauysche a pore man; for to rauysche a pore man, while he drawith the pore man.
10 Anthuwo amawapondaponda ndipo amakomoka; amakhala pansi pa mphamvu zake.
In his snare he schal make meke the pore man; he schal bowe hym silf, and schal falle doun, whanne he hath be lord of pore men.
11 Iye amati mu mtima mwake, “Mulungu wayiwala, wabisa nkhope yake ndipo sakuonanso.”
For he seide in his herte, God hath foryete; he hath turned awei his face, that he se not in to the ende.
12 Dzukani Yehova! Onetsani dzanja lanu Inu Mulungu. Musayiwale anthu opanda mphamvu.
Lord God, rise thou vp, and thin hond be enhaunsid; foryete thou not pore men.
13 Nʼchifukwa chiyani munthu woyipa amachitira chipongwe Mulungu? Chifukwa chiyani amati mu mtima mwake, “Iye sandiyimba mlandu?”
For what thing terride the wickid man God to wraththe? for he seide in his herte, God schal not seke.
14 Komatu Inu Mulungu, mumazindikira mavuto ndi zosautsa, mumaganizira zochitapo kanthu. Wovutikayo amadzipereka yekha kwa Inu pakuti Inu ndi mthandizi wa ana amasiye.
Thou seest, for thou biholdist trauel and sorewe; that thou take hem in to thin hondis. The pore man is left to thee; thou schalt be an helpere to the fadirles and modirles.
15 Thyolani dzanja la woyipitsitsa ndi la munthu woyipa; muzengeni mlandu chifukwa cha zoyipa zake zimene sizikanadziwika.
Al to-breke thou the arme of the synnere, and yuel willid; his synne schal be souyt, and it schal not be foundun.
16 Yehova ndi Mfumu kwamuyaya; mitundu ya anthu idzawonongeka kuchoka mʼdziko lake.
The Lord schal regne with outen ende, and in to the world of world; folkis, ye schulen perische fro the lond of hym.
17 Mumamva Inu Yehova, zokhumba za osautsidwa; mumawalimbikitsa ndipo mumamva kulira kwawo.
The Lord hath herd the desir of pore men; thin eere hath herd the makyng redi of her herte.
18 Kuteteza ana amasiye ndi oponderezedwa, ndi cholinga chakuti munthu amene ali wa dziko lapansi asaopsenso.
To deme for the modirles `and meke; that a man `leie to no more to `magnyfie hym silf on erthe.

< Masalimo 10 >