< Masalimo 10 >

1 Nʼchifukwa chiyani Yehova mwayima patali? Chifukwa chiyani mukudzibisa nokha pa nthawi ya mavuto?
Why standest thou afar off, O LORD? Why hidest thou thyself in times of trouble?
2 Mwa kunyada kwake munthu woyipa asaka wofowoka, amene akodwa mʼnjira zimene iye wakonza.
Through the haughtiness of the wicked the poor are in distress; They are caught in the wiles which are contrived for them.
3 Iye amatamandira zokhumba za mu mtima wake; amadalitsa aumbombo ndi kuchitira chipongwe Yehova.
The wicked boasteth of his heart's desire; The rapacious renounceth and contemneth Jehovah.
4 Mwa kunyada kwake woyipa safunafuna Mulungu; mʼmaganizo ake wonse mulibe malo a Mulungu.
The wicked [[saith]] in his haughtiness, “He careth not!” All his thoughts are, “There is no God.”
5 Zinthu zake zimamuyendera bwino; iye ndi wamwano ndipo malamulo anu ali nawo kutali; amanyogodola adani ake onse.
His course is always prosperous; Far in the heights are thy judgments from him; As for all his enemies, he puffeth at them.
6 Iye amadziyankhulira kuti, “Palibe chimene chidzandigwedeze. Ndidzakhala wokondwa nthawi zonse ndipo sindidzakhala pa mavuto.”
He saith in his heart, “I shall never fall; I shall never be in adversity.”
7 Mʼkamwa mwake mwadzaza matemberero, mabodza ndi zoopseza; zovutitsa ndi zoyipa zili pansi pa lilime lake.
His mouth is full of perjury, deceit, and oppression; Mischief and injustice are upon his tongue.
8 Iye amabisalira anthu pafupi ndi midzi, kuchokera pobisalapo amapha anthu osalakwa, amayangʼanayangʼana mwachinsinsi anthu oti awawononge.
He sitteth in the lurking-places of the villages; In secret places doth he murder the innocent; His eyes are secretly fixed upon the poor.
9 Amabisalira anthu ngati mkango pa zitsamba. Amabisalira kuti agwire anthu opanda mphamvu; amagwira anthu opanda mphamvu ndi kuwakokera mu ukonde wake.
He secretly lieth in wait, like a lion in a thicket; He lieth in wait to seize upon the helpless; He catcheth the poor, drawing him into his net.
10 Anthuwo amawapondaponda ndipo amakomoka; amakhala pansi pa mphamvu zake.
He croucheth, and lowereth himself, And the wretched fall into his paws.
11 Iye amati mu mtima mwake, “Mulungu wayiwala, wabisa nkhope yake ndipo sakuonanso.”
He saith in his heart, “God doth forget; He hideth his face; he doth never see it.”
12 Dzukani Yehova! Onetsani dzanja lanu Inu Mulungu. Musayiwale anthu opanda mphamvu.
Arise, O LORD! O God, lift up thine hand: Forget not the distressed!
13 Nʼchifukwa chiyani munthu woyipa amachitira chipongwe Mulungu? Chifukwa chiyani amati mu mtima mwake, “Iye sandiyimba mlandu?”
Wherefore doth the wicked contemn God, And say in his heart, “He careth not for it”?
14 Komatu Inu Mulungu, mumazindikira mavuto ndi zosautsa, mumaganizira zochitapo kanthu. Wovutikayo amadzipereka yekha kwa Inu pakuti Inu ndi mthandizi wa ana amasiye.
Thou dost see it; yea, thou beholdest malice and oppression, And markest it upon thy hand! The poor committeth himself to thee; Thou art the helper of the fatherless.
15 Thyolani dzanja la woyipitsitsa ndi la munthu woyipa; muzengeni mlandu chifukwa cha zoyipa zake zimene sizikanadziwika.
Break thou the arm of the unjust and wicked man; Seek out his wickedness, till thou canst find none!
16 Yehova ndi Mfumu kwamuyaya; mitundu ya anthu idzawonongeka kuchoka mʼdziko lake.
Jehovah is king for ever and ever; The gentiles shall perish out of his land.
17 Mumamva Inu Yehova, zokhumba za osautsidwa; mumawalimbikitsa ndipo mumamva kulira kwawo.
Thou, O LORD! wilt hear the desires of the distressed; Thou wilt strengthen their hearts; Thou wilt lend a listening ear!
18 Kuteteza ana amasiye ndi oponderezedwa, ndi cholinga chakuti munthu amene ali wa dziko lapansi asaopsenso.
Thou wilt maintain the cause of the fatherless and the oppressed, That henceforth none may be driven from the land.

< Masalimo 10 >