< Masalimo 1 >

1 Wodala munthu amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa, kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa, kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
Ubusisiwe umuntu ongahambi ngeseluleko sababi, ongemi endleleni yezoni, ongahlali esihlalweni sabagconayo;
2 Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
kodwa intokozo yakhe isemlayweni weNkosi, uzindla ngomlayo wayo emini lebusuku.
3 Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake ndipo masamba ake safota. Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
Njalo uzakuba njengesihlahla esihlanyelwe emifuleni yamanzi, esithela isithelo saso ngesikhathi saso, ohlamvu laso kaliyikubuna; lakho konke akwenzayo kuzaphumelela.
4 Sizitero ndi anthu oyipa! Iwo ali ngati mungu umene umawuluzidwa ndi mphepo.
Ababi kabanjalo, kodwa banjengamakhoba umoya owaphephulayo.
5 Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo, kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.
Ngakho ababi kabayikuma ekwahlulelweni, lezoni enhlanganweni yabalungileyo.
6 Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama, koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.
Ngoba iNkosi iyayazi indlela yabalungileyo, kodwa indlela yababi izabhubha.

< Masalimo 1 >