< Masalimo 1 >
1 Wodala munthu amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa, kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa, kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
Heureux l'homme qui ne suit pas les conseils des méchants, ni se tenir sur le chemin des pécheurs, ni s'asseoir sur le siège des moqueurs;
2 Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
mais son plaisir est dans la loi de Yahvé. Il médite jour et nuit sur sa loi.
3 Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake ndipo masamba ake safota. Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
Il sera comme un arbre planté près des ruisseaux d'eau, qui produit son fruit en sa saison, dont la feuille ne se fane pas non plus. Tout ce qu'il fait sera prospère.
4 Sizitero ndi anthu oyipa! Iwo ali ngati mungu umene umawuluzidwa ndi mphepo.
Les méchants ne sont pas ainsi, mais sont comme la paille que le vent chasse.
5 Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo, kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.
C'est pourquoi les méchants ne tiendront pas dans le jugement, ni les pécheurs dans la congrégation des justes.
6 Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama, koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.
Car Yahvé connaît la voie des justes, mais la voie des méchants périra.