< Masalimo 1 >

1 Wodala munthu amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa, kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa, kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
Happy are those who don't follow the advice of the wicked. They refuse to adopt the ways of sinful people, and they don't make fun of others.
2 Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
Instead they love to do what the law of the Lord says, and they think about it day and night.
3 Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake ndipo masamba ake safota. Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
They're like trees growing by flowing rivers, producing fruit every season. Their leaves never wither, and they are successful in all they do.
4 Sizitero ndi anthu oyipa! Iwo ali ngati mungu umene umawuluzidwa ndi mphepo.
But it's not like that for the wicked! They are like chaff, blown away by the wind.
5 Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo, kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.
For this reason the wicked will not survive the judgment—sinners have no place among those who live right.
6 Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama, koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.
For the Lord watches over those who follow the right way, but the way of the wicked leads to death.

< Masalimo 1 >