< Miyambo 1 >
1 Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
Izaga zikaSolomoni indodana kaDavida, inkosi yako-Israyeli:
2 Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
ukuba abantu bazuze ukuhlakanipha lokuzithiba; ukuba bazwisise amazwi okuqedisisa;
3 kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
ukuba bazuze impilo yokuzithiba lobuqotho, besenza okulungileyo, okufaneleyo lokuqondileyo;
4 Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
ukunika ulwazi kwabayizithutha, ulwazi lokukhetha okuqondileyo kwabatsha
5 Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
ukuthi ohlakaniphileyo alalele engeze ukufunda kwakhe, kuthi obonisisayo azuze izeluleko,
6 kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
ukuba abantu bazwisise izaga lemizekeliso, izitsho lamalibho abahlakaniphileyo.
7 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
Ukwesaba uThixo kuyikuqala kwenhlakanipho, kodwa iziwula ziyakweyisa ukuqedisisa lokuzithiba.
8 Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
Lalela, ndodana yami, izeluleko zikayihlo njalo ungadeli imfundiso kanyoko.
9 Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
Kuzakuba ngumqhele omuhle ekhanda lakho lomgaxo wokucecisa intamo yakho.
10 Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
Ndodana yami, aluba izoni zikuhuga, ungaze wavuma.
11 Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
Nxa zisithi, “Woza sihambe; kasicathamele abantu sichithe igazi, kasicwathele omunye umuntu ongelacala;
12 tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol )
kasibaginye bephila njengengcwaba, sibajwamule njengabawele emgodini; (Sheol )
13 Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
sizazuza impahla ezinhle ezehlukeneyo sigcwalise izindlu zethu ngempango;
14 Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
phathisana lathi ukuze sibelesikhwama sinye”
15 Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
ndodana yami, ungahambi lazo, ungalugxobi olwakho ezindleleni zazo;
16 Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
ngoba ezabo inyawo zigijima ekoneni, bachitha igazi lula.
17 Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
Kakusizi ukuthiya ngembule lithe dandalazi emehlweni ezinyoni!
18 Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
Abantu laba bacathamela ukuchitheka kwelabo igazi; bajuma okwabo ukuphila.
19 Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
Sinjalo isiphetho salabo abadinga inzuzo ngobugebenga; kuyayichitha impilo yalabo abayitholayo.
20 Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
Ukuhlakanipha kuyamemeza emgwaqweni, kuphakamisa ilizwi lakho ezinkundleni;
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
kuyanqongoloza lezindleleni okuxokozela khona, kuyatshumayela emasangweni omuzi kuthi:
22 “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
“Koze kube nini lina zithutha lithanda ubuthutha benu na? Koze kube nini izideleli zikholisa ukudelela leziphukuphuku zizonda ulwazi na?
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
Lalelani ukukhuza kwami liphenduke! Ngizalivulela isifuba sami, ngilivezele imicabango yami.
24 Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
Kodwa ngenxa yokuthi langifulathela ngilibiza, kwangabi khona onginanzayo ngiselula isandla sami,
25 Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
njengoba lala izeluleko zami njalo kalavuma ukukhuza kwami,
26 Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
ngakho lami ngizahleka selihlupheka; ngizaliklolodela nxa lisehlelwa lusizi,
27 Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
nxa usizi lulehlela njengesiphepho; nxa incithakalo ilikhukhula njengesivunguzane, nxa usizi lezinhlupheko ziligabhela.
28 “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
Lapho-ke bazangibiza kodwa kangiyikusabela; bazangidinga bangangitholi.
29 Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
Ngoba babeluzonda ulwazi kabaze bakhetha ukwesaba uThixo
30 popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
ngoba kabavumanga iseluleko sami, badelela ukukhuza kwami,
31 Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
bazakudla izithelo zokuhamba kwabo basuthiswe ngezithelo zamacebo abo.
32 Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
Phela ubuhlongandlebe bezithutha buzazibulala, lokungananzi kweziphukuphuku kuzazibhubhisa;
33 Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”
kodwa lowo ongilalelayo uzahlala evikelekile ekhululekile, engesabi lutho olungamlimaza.”