< Miyambo 1 >

1 Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
[Parabolæ Salomonis, filii David, regis Israël,
2 Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
ad sciendam sapientiam et disciplinam;
3 kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
ad intelligenda verba prudentiæ, et suscipiendam eruditionem doctrinæ, justitiam, et judicium, et æquitatem:
4 Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
ut detur parvulis astutia, adolescenti scientia et intellectus.
5 Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
Audiens sapiens, sapientior erit, et intelligens gubernacula possidebit.
6 kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
Animadvertet parabolam et interpretationem, verba sapientum et ænigmata eorum.
7 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
Timor Domini principium sapientiæ; sapientiam atque doctrinam stulti despiciunt.]
8 Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
[Audi, fili mi, disciplinam patris tui, et ne dimittas legem matris tuæ:
9 Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
ut addatur gratia capiti tuo, et torques collo tuo.
10 Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
Fili mi, si te lactaverint peccatores, ne acquiescas eis.
11 Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
Si dixerint: Veni nobiscum, insidiemur sanguini; abscondamus tendiculas contra insontem frustra;
12 tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
deglutiamus eum sicut infernus viventem, et integrum quasi descendentem in lacum; (Sheol h7585)
13 Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
omnem pretiosam substantiam reperiemus; implebimus domos nostras spoliis:
14 Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
sortem mitte nobiscum, marsupium unum sit omnium nostrum:
15 Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
fili mi, ne ambules cum eis; prohibe pedem tuum a semitis eorum:
16 Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
pedes enim illorum ad malum currunt, et festinant ut effundant sanguinem.
17 Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
Frustra autem jacitur rete ante oculos pennatorum.
18 Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
Ipsi quoque contra sanguinem suum insidiantur, et moliuntur fraudes contra animas suas.
19 Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
Sic semitæ omnis avari: animas possidentium rapiunt.]
20 Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
[Sapientia foris prædicat; in plateis dat vocem suam:
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
in capite turbarum clamitat; in foribus portarum urbis profert verba sua, dicens:
22 “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
Usquequo, parvuli, diligitis infantiam, et stulti ea quæ sibi sunt noxia cupient, et imprudentes odibunt scientiam?
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
convertimini ad correptionem meam. En proferam vobis spiritum meum, et ostendam vobis verba mea.
24 Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
Quia vocavi, et renuistis; extendi manum meam, et non fuit qui aspiceret:
25 Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
despexistis omne consilium meum, et increpationes meas neglexistis.
26 Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
Ego quoque in interitu vestro ridebo, et subsannabo cum vobis id quod timebatis advenerit.
27 Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
Cum irruerit repentina calamitas, et interitus quasi tempestas ingruerit; quando venerit super vos tribulatio et angustia:
28 “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
tunc invocabunt me, et non exaudiam; mane consurgent, et non invenient me:
29 Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
eo quod exosam habuerint disciplinam, et timorem Domini non susceperint,
30 popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
nec acquieverint consilio meo, et detraxerint universæ correptioni meæ.
31 Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
Comedent igitur fructus viæ suæ, suisque consiliis saturabuntur.
32 Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
Aversio parvulorum interficiet eos, et prosperitas stultorum perdet illos.
33 Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”
Qui autem me audierit, absque terrore requiescet, et abundantia perfruetur, timore malorum sublato.]

< Miyambo 1 >