< Miyambo 1 >
1 Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
Sprüche Salomos, des Sohnes Davids, des Königs von Israel,
2 Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
daß man Weisheit und Zucht erlerne und verständige Reden verstehe,
3 kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
daß man Gedankenzucht erlange, Rechtssinn, Urteilskraft und Aufrichtigkeit;
4 Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
damit den Einfältigen Klugheit, den Jünglingen Erkenntnis und Besonnenheit verliehen werde.
5 Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
Wer weise ist, hört darauf und vermehrt seine Kenntnisse, und wer verständig ist, eignet sich Fertigkeiten an,
6 kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
damit er Sprichwörter und bildliche Rede verstehe, die Worte der Weisen und ihre Rätsel.
7 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
Die Furcht des HERRN ist der Anfang der Erkenntnis; nur Toren verachten Weisheit und Zucht!
8 Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
Höre, mein Sohn, die Unterweisung deines Vaters und verwirf nicht die Lehre deiner Mutter!
9 Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
Denn sie sind ein schöner Kranz für dein Haupt und ein Geschmeide um deinen Hals.
10 Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
Mein Sohn, wenn dich Sünder überreden wollen, so willige nicht ein,
11 Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
wenn sie sagen: «Komm mit uns, wir wollen auf Blut lauern, wir wollen dem Unschuldigen ohne Ursache nachstellen;
12 tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol )
wir wollen sie verschlingen wie der Scheol die Lebendigen, als sänken sie unversehens ins Grab! (Sheol )
13 Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
Wir wollen allerlei kostbares Gut gewinnen und unsre Häuser füllen mit Raub;
14 Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
schließe dich uns auf gut Glück an, wir wollen gemeinsame Kasse führen!»
15 Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
Mein Sohn, geh nicht mit ihnen auf dem Wege, halte deinen Fuß zurück von ihrem Pfad!
16 Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
Denn ihre Füße laufen zum Bösen und eilen Blut zu vergießen.
17 Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
Denn vergeblich wird das Netz ausgespannt vor den Augen aller Vögel;
18 Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
sie aber lauern auf ihr eigenes Blut und stellen ihrem eigenen Leben nach.
19 Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
Dies ist das Schicksal aller, die nach [ungerechtem] Gewinn trachten: er kostet seinen Besitzern die Seele!
20 Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
Die Weisheit ruft draußen laut, öffentlich läßt sie ihre Stimme hören;
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
im ärgsten Straßenlärm schreit sie, an den Pforten der Stadttore hält sie ihre Reden:
22 “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
Wie lange wollt ihr Einfältigen die Einfalt lieben und ihr Spötter Lust am Spotten haben und ihr Toren Erkenntnis hassen?
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
Kehret um zu meiner Zurechtweisung! Siehe, ich will euch meinen Geist sprudeln lassen, euch meine Worte kundtun!
24 Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
Darum, weil ich rufe und ihr mich abweiset, weil ich meine Hand ausstrecke und niemand darauf achtet,
25 Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
weil ihr vielmehr allen meinen Rat verwerfet und meine Zurechtweisung nicht begehret,
26 Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
so werde auch ich eures Unglücks lachen und euer spotten,
27 Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
wenn das, was ihr fürchtet, wie ein Wetter über euch kommt und euer Schicksal euch wie ein Wirbelsturm überraschen wird, wenn euch Angst und Not überfällt.
28 “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
Dann werden sie mich anrufen, aber ich werde nicht antworten; sie werden mich eifrig suchen und nicht finden,
29 Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
darum, daß sie die Erkenntnis gehaßt und die Furcht des HERRN nicht erwählt haben,
30 popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
daß sie meinen Rat nicht begehrt und alle meine Zurechtweisung verschmäht haben.
31 Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
Darum sollen sie von der Frucht ihres eigenen Weges essen und von ihren eigenen Ratschlägen genug bekommen!
32 Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
Denn ihre Verirrung bringt die Einfältigen um, und ihre Sorglosigkeit stürzt die Toren ins Verderben.
33 Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”
Wer aber mir gehorcht, wird sicher wohnen und kein Unheil fürchten müssen.