< Miyambo 1 >
1 Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
Proverbes de Salomon, fils de David, roi d'Israël;
2 Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
Pour faire connaître la sagesse et l'instruction, pour faire comprendre les discours d'intelligence;
3 kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
Pour faire recevoir une instruction de raison, de justice, de jugement, et d'équité;
4 Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
Pour donner du discernement aux simples, de la connaissance et de la réflexion au jeune homme.
5 Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
Le sage écoutera et deviendra plus instruit, et l'homme intelligent acquerra de la prudence,
6 kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
Afin d'entendre les sentences et les énigmes, les paroles des sages, et leurs discours profonds.
7 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
La crainte de l'Éternel est le principal point de la science; mais les fous méprisent la sagesse et l'instruction.
8 Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
Mon fils, écoute l'instruction de ton père, et n'abandonne point l'enseignement de ta mère.
9 Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
Car ce sont des grâces assemblées autour de ta tête, et des colliers à ton cou.
10 Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
Mon fils, si les pécheurs veulent te séduire, n'y consens pas.
11 Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
S'ils disent: Viens avec nous, dressons des embûches pour tuer; tendons des pièges à l'innocent, sans qu'il en ait donné de sujet;
12 tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol )
Engloutissons-les tout vifs comme le Sépulcre, et tout entiers comme ceux qui descendent dans la fosse; (Sheol )
13 Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
Nous trouverons toutes sortes de biens précieux, nous remplirons nos maisons de butin;
14 Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
Tu y auras ta part avec nous, il n'y aura qu'une bourse pour nous tous.
15 Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
Mon fils, ne te mets point en chemin avec eux; détourne ton pied de leur sentier.
16 Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
Car leurs pieds courent au mal, et ils se hâtent pour répandre le sang.
17 Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
Or c'est en vain qu'on tend le filet devant les yeux de tout ce qui a des ailes;
18 Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
Mais eux, ils dressent des embûches contre leur propre sang, et ils tendent des pièges à leur âme.
19 Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
Telles sont les voies de celui qui convoite le gain déshonnête, lequel perdra l'âme de ceux qui le poursuivent.
20 Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
La souveraine sagesse crie hautement par les rues, elle fait retentir sa voix sur les places;
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
Elle crie dans les carrefours, où on fait le plus de bruit, aux entrées des portes; elle prononce ses paroles par la ville:
22 “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
Stupides, dit-elle, jusques à quand aimerez-vous la sottise? Jusques à quand les moqueurs prendront-ils plaisir à la moquerie, et les insensés auront-ils en haine la science?
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
Étant repris par moi, convertissez-vous. Voici, je vous communiquerai de mon esprit en abondance, je vous ferai comprendre mes paroles.
24 Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
Puisque j'ai crié, et que vous avez refusé d'entendre; que j'ai étendu ma main, et que personne n'y a pris garde;
25 Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
Puisque vous rejetez tous mes conseils, et que vous n'aimez pas mes réprimandes,
26 Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
Je me rirai, moi, de votre calamité, je me moquerai quand votre effroi surviendra;
27 Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
Quand votre effroi surviendra comme une ruine, et votre calamité comme une tempête; quand la détresse et l'angoisse viendront sur vous.
28 “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
Alors ils crieront vers moi, mais je ne répondrai point; ils me chercheront de grand matin, mais ils ne me trouveront point;
29 Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
Parce qu'ils ont haï la science, et qu'ils n'ont point choisi la crainte de l'Éternel.
30 popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
Ils n'ont point pris plaisir à mon conseil; ils ont dédaigné toutes mes réprimandes.
31 Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
Qu'ils mangent donc le fruit de leur voie, et qu'ils se rassasient de leurs conseils.
32 Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
Car l'égarement des sots les tue, et la sécurité des insensés les perd.
33 Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”
Mais celui qui m'écoute, habitera en sûreté, et sera tranquille, sans être effrayé d'aucun mal.