< Miyambo 1 >

1 Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
The wise sayings of Solomon, the son of David, king of Israel.
2 Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
To have knowledge of wise teaching; to be clear about the words of reason:
3 kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
To be trained in the ways of wisdom, in righteousness and judging truly and straight behaviour:
4 Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
To make the simple-minded sharp, and to give the young man knowledge, and serious purpose:
5 Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
(The wise man, hearing, will get greater learning, and the acts of the man of good sense will be wisely guided: )
6 kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
To get the sense of wise sayings and secrets, and of the words of the wise and their dark sayings.
7 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
The fear of the Lord is the start of knowledge: but the foolish have no use for wisdom and teaching.
8 Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
My son, give ear to the training of your father, and do not give up the teaching of your mother:
9 Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
For they will be a crown of grace for your head, and chain-ornaments about your neck.
10 Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
My son, if sinners would take you out of the right way, do not go with them.
11 Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
If they say, Come with us; let us make designs against the good, waiting secretly for the upright, without cause;
12 tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
Let us overcome them living, like the underworld, and in their strength, as those who go down to death; (Sheol h7585)
13 Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
Goods of great price will be ours, our houses will be full of wealth;
14 Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
Take your chance with us, and we will all have one money-bag:
15 Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
My son, do not go with them; keep your feet from their ways:
16 Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
For their feet are running after evil, and they are quick to take a man's life.
17 Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
Truly, to no purpose is the net stretched out before the eyes of the bird:
18 Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
And they are secretly waiting for their blood and making ready destruction for themselves.
19 Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
Such is the fate of everyone who goes in search of profit; it takes away the life of its owners.
20 Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
Wisdom is crying out in the street; her voice is loud in the open places;
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
Her words are sounding in the meeting-places, and in the doorways of the town:
22 “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
How long, you simple ones, will foolish things be dear to you? and pride a delight to the haters of authority? how long will the foolish go on hating knowledge?
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
Be turned again by my sharp words: see, I will send the flow of my spirit on you, and make my words clear to you.
24 Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
Because your ears were shut to my voice; no one gave attention to my out-stretched hand;
25 Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
You were not controlled by my guiding, and would have nothing to do with my sharp words:
26 Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
So in the day of your trouble I will be laughing; I will make sport of your fear;
27 Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
When your fear comes on you like a storm, and your trouble like a rushing wind; when pain and sorrow come on you.
28 “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
Then I will give no answer to their cries; searching for me early, they will not see me:
29 Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
For they were haters of knowledge, and did not give their hearts to the fear of the Lord:
30 popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
They had no desire for my teaching, and my words of protest were as nothing to them.
31 Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
So the fruit of their way will be their food, and with the designs of their hearts they will be made full.
32 Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
For the turning back of the simple from teaching will be the cause of their death, and the peace of the foolish will be their destruction.
33 Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”
But whoever gives ear to me will take his rest safely, living in peace without fear of evil.

< Miyambo 1 >