< Miyambo 1 >

1 Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
Israel sangpahrang David a capa Solomon ak awicyih taw;
2 Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
Cyihnaak ingkaw cawngpyinaak, zaaksimnaak thaikhqi siimsak ham,
3 kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
Dyngnaak, awitlyknaak, pekbonaak a awm kaana hawnaak thai ham ingkaw cawngpyinaak ak thym pawmnaak thai ham;
4 Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
Khawk hangkhqi khawsimnaak taaksak ham ingkaw, cacoenkhqi khawkpoek thainaak taaksak ham;
5 Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
Thlakcyikhqi ing siim unawh a mi cyihnaak a pungnaak khqoet nawh, khawkpoek thaikhqi ing khawkpoeknaak thai a mi taaknaak khqoet hamna,
6 kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
Awicyih ingkaw ak kqawncaihnaakkhqi, thlakcyi ak awi ingkaw a mik awih kqawn zaaksimnaak thai nace awm hy.
7 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
Bawipa kqihchahnaak taw cyihnaak a kungpyina awm nawh; Cehlai, thlakqawkhqi ingtaw cyihnaak ingkaw cawngpyinaak husit uhy.
8 Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
Ka capa, na pa cawngpyinaak ce ngai nawh, na nu cawngpyinaak ce koeh hoet.
9 Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
Na lu hamna khqaipai leek soeihna awm nawh, na hawng hamna aawi hun leek soeihna awm kaw.
10 Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
Ka capa, thlakchekhqi ing a ni zoek awh koeh ngai kawp ti.
11 Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
“Kami venna law lah, thlang a thi lawng sak lah usih, thlakche ak qeenkhqi ce qym khqi lah usih;
12 tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
Ceikhui amyihna a hqingpumna daih khqi lah usih, phyi khui amyihna. (Sheol h7585)
13 Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
A phuk tlotlokhqi ni ham kawm saw, thlang a theem ni qawtkhqi ing ni im ce nik bee kaw.
14 Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
“Kami venawh bang lawlawt nawh taw, tangka bawm ni qup haih kawm uh,” a mi ti awh,
15 Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
Ka capa, a ming lakawh koeh boei nawh, a mi lam awhkawng phleng qu kawp ti.
16 Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
A mi khaw ce thawlhnaak lam benna kaan unawh, thi ak lawngsak hamna a ming hqii tawn sak uhy.
17 Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
Lawk ce ak chaap maina zan ni, kawmyih phaa a haiawh awm.
18 Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
Cekkhqi taw a mimah thi ce lawngsak unawh a mi hqingnaak ak plamsakkhqi ni.
19 Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
Ceamyihna ni, a mak thymna ak kamvaakhqi lam taw; ami boei a hqingnaak ce lawh pe uhy.
20 Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
Chawmkeeng awh cyihnaak ce khawteh na khyy nawh, Chawmkeeng tung keengawh ce khyy hy;
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
Thlang khawzah ang cunnaak ang lungkil awh ce khyy nawh, khawkkhui lutnaak vawng chawmkeeng awhce khyy hy.
22 “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
Nangmih khawk hangkhqi aw, i qyt dy nu khaw na mi hang hly? I qyt dy nu a nik husit khqi huhsitnaak khuiawh na mi awm hly, thlakqawkhqi ing cyihnaak na mi maa hly?
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
Ka ni toelnaakkhqi benna voei law uh: Ngai lah uh, na mik khanawh kang myihla theeh kawng nyng saw, kak awi zaaksimnaak ni pekkhqi kawng.
24 Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
Nik khykhqi nyng, ni maa uhyk ti, ka kut soeng nyng, uca ingawm am do uhyk ti;
25 Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
Ka khawkhannaakkhqi boeih ikawna am ngai unawh, ka ni toelnaakkhqi boeih ce hooet uhyk ti.
26 Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
Ceamyihna awmsaw, kai ingawm na mi zoseet nyn awh ni qaih nak khqi kawng nyng saw, kyinaak na mi sawng lawawh ni qaih nak khqi kawng nyng.
27 Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
Na mi lynak hlinu amyihna a thoeng law nawh, na mi zoseetnaak tym ing a pha lawawh, kyinaak ingkaw ngaihangnaak namik khanawh a pha law awh.
28 “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
Chawh ce, nik khy kawm uh tik saw, cesei-awm am nim hlat khqi kawng: mymcang hii awh ni sui kawm uk tik saw, ceseiawm am ni hu kawm uk ti;
29 Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
Cyihnaak maa unawh, Bawipa kqihchahnaak ce ama mik tyhnaak ak caming.
30 popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
Ka khawkhannaak pynoet ca mai awm am ngaih unawh, ka toelthamnaak boeih ce a mi huhsit caming.
31 Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
Ceamyihna awmsaw a mi khawsak ak thaih qah ce aii kawm usaw, a mik poeknaak ing qoh kawm uh.
32 Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
Thlakchekhqi hu benna nawngnaak ing a mimah him khqi kawm saw, ak qawkhqi ang ngaihdingnaak ing amimah moeng sak khqi kaw.
33 Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”
Kak awi ak haanaak taw ak ding cana khaw sa kawm usaw, zoseetnaak khuiawh awm ngaiqeep cana khawsa kawm uh.

< Miyambo 1 >