< Miyambo 9 >
1 Nzeru inamanga nyumba yake; inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.
Danaliⱪ ɵzigǝ bir ɵy selip, Uning yǝttǝ tüwrükini ornatti.
2 Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake; inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.
U mallirini soyup, Esil xarablirini arilaxturup tǝyyarlap, Ziyapǝt dastihinini yaydi;
3 Nzeruyo inatuma adzakazi ake, kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,
Dedǝklirini [meⱨman qaⱪirixⱪa] ǝwǝtti, Ɵzi xǝⱨǝrning ǝng egiz jaylirida turup:
4 “Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!” Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,
«I saddilar, bu yǝrgǝ kelinglar, — dǝp qaⱪiriwatidu; Nadanlarƣa:
5 “Bwerani, dzadyeni chakudya changa ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.
Ⱪeni, nanlirimdin eƣiz tegip, Mǝn arilaxturup tǝyyarliƣan xarablardin iqinglar;
6 Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo; yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”
Nadanlar ⱪataridin qiⱪip, ⱨayatⱪa erixinglar, Yoruⱪluⱪ yolida menginglar», — dǝwatidu.
7 Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo; aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.
Ⱨakawurlarƣa tǝnbiⱨ bǝrgüqi aⱨanǝtkǝ uqraydu, Ⱪǝbiⱨlǝrni ǝyibligüqi ɵzigǝ daƣ kǝltüridu.
8 Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe; dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.
Ⱨakawurlarni ǝyiblimǝ, qünki u sanga ɵq bolup ⱪalidu; Ⱨalbuki, dana kixini ǝyiblisǝng, u seni sɵyidu.
9 Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru; ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.
Dana adǝmgǝ dǝwǝt ⱪilsang, ǝⱪli tehimu toluⱪ bolidu; Ⱨǝⱪⱪaniy adǝmgǝ durus yol kɵrsǝtsǝng, Bilimi tehimu axidu.
10 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru; kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.
Pǝrwǝrdigardin ǝyminix danaliⱪning baxlinixidur, Muⱪǝddǝs bolƣuqini tonux yoruⱪluⱪtur.
11 Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka, ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.
Mǝn [danaliⱪ] sǝndǝ bolsam, künliringni uzartimǝn, Ɵmrüngning yilliri kɵpiyǝr.
12 Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa; ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.
Sǝndǝ danaliⱪ bolsa, paydini kɵridiƣan ɵzüngsǝn, Danaliⱪni mazaⱪ ⱪilsang ziyan tartidiƣanmu ɵzüngsǝn.
13 Uchitsiru ndi mkazi waphokoso, wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.
Nadan hotun aƣzi bisǝrǝmjan, ǝⱪilsizdur, Ⱨeqnemǝ bilmǝstur.
14 Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake, pamalo aatali a mu mzinda,
U ixik aldida olturup, Xǝⱨǝrning ǝng egiz jaylirida orun elip,
15 kuti aziyitana anthu ongodutsa, amene akunka nayenda njira zawo.
Udul ɵtüp ketiwatⱪanlarƣa:
16 Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,” ndipo kwa wopanda nzeru amati,
«Kimki sadda bolsa, bu yǝrgǝ kǝlsun!» — dǝwatidu, Wǝ ǝⱪilsizlǝrni:
17 “Madzi akuba ndiye amatsekemera; chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”
«Oƣriliⱪqǝ iqkǝn su tatliⱪ bolidu, Oƣrilap yegǝn nan tǝmlik bolidu!» — dǝp qarⱪiwatidu.
18 Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko, ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya. (Sheol )
Lekin qaⱪirilƣuqi ɵlüklǝrning uning ɵyidǝ yatⱪanliⱪidin bihǝwǝrdur, Uning [burunⱪi] meⱨmanlirining alliⱪaqan tǝⱨtisaraning tǝglirigǝ qüxüp kǝtkǝnlikini u sǝzmǝs. (Sheol )