< Miyambo 9 >

1 Nzeru inamanga nyumba yake; inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.
Premudrost sazida sebi kuæu, i otesa sedam stupova;
2 Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake; inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.
Pokla stoku svoju, rastvori vino svoje, i postavi sto svoj.
3 Nzeruyo inatuma adzakazi ake, kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,
Posla djevojke svoje, te zove svrh visina gradskih:
4 “Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!” Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,
Ko je lud, neka se uvrati ovamo. I bezumnima veli:
5 “Bwerani, dzadyeni chakudya changa ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.
Hodite, jedite hljeba mojega, i pijte vina koje sam rastvorila.
6 Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo; yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”
Ostavite ludost i biæete živi, i idite putem razuma.
7 Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo; aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.
Ko uèi potsmjevaèa, prima sramotu; i ko kori bezbožnika, prima rug.
8 Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe; dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.
Ne karaj potsmjevaèa da ne omrzne na te; karaj mudra, i ljubiæe te.
9 Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru; ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.
Kaži mudrome, i biæe još mudriji; pouèi pravednoga, i znaæe više.
10 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru; kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.
Poèetak je mudrosti strah Gospodnji, i znanje je svetijeh stvari razum.
11 Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka, ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.
Jer æe se mnom umnožiti dani tvoji i dodaæe ti se godine životu.
12 Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa; ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.
Ako budeš mudar, sebi æeš biti mudar; ako li budeš potsmjevaè, sam æeš tegliti.
13 Uchitsiru ndi mkazi waphokoso, wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.
Žena bezumna plaha je, luda i ništa ne zna;
14 Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake, pamalo aatali a mu mzinda,
I sjedi na vratima od kuæe svoje na stolici, na visinama gradskim,
15 kuti aziyitana anthu ongodutsa, amene akunka nayenda njira zawo.
Te vièe one koji prolaze, koji idu pravo svojim putem:
16 Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,” ndipo kwa wopanda nzeru amati,
Ko je lud? neka se uvrati ovamo. I bezumnome govori:
17 “Madzi akuba ndiye amatsekemera; chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”
Voda je kradena slatka, i hljeb je sakriven ugodan.
18 Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko, ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya. (Sheol h7585)
A on ne zna da su ondje mrtvaci i u dubokom grobu da su zvanice njezine. (Sheol h7585)

< Miyambo 9 >