< Miyambo 9 >

1 Nzeru inamanga nyumba yake; inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.
حکمت، خانه خود را بنا کرده، و هفت ستونهای خویش را تراشیده است.۱
2 Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake; inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.
ذبایح خود را ذبح نموده و شراب خود را ممزوج ساخته و سفره خود را نیز آراسته است.۲
3 Nzeruyo inatuma adzakazi ake, kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,
کنیزان خود را فرستاده، ندا کرده است، بر پشتهای بلندشهر.۳
4 “Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!” Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,
هر‌که جاهل باشد به اینجا بیاید، و هر‌که ناقص العقل است او را می‌گوید.۴
5 “Bwerani, dzadyeni chakudya changa ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.
بیایید از غذای من بخورید، و از شرابی که ممزوج ساخته‌ام بنوشید.۵
6 Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo; yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”
جهالت را ترک کرده، زنده بمانید، و به طریق فهم سلوک نمایید.۶
7 Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo; aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.
هر‌که استهزاکننده راتادیب نماید، برای خویشتن رسوایی را تحصیل کند، و هر‌که شریر را تنبیه نماید برای او عیب می‌باشد.۷
8 Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe; dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.
استهزاکننده را تنبیه منما مبادا از تونفرت کند، اما مرد حکیم را تنبیه نما که تو رادوست خواهد داشت.۸
9 Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru; ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.
مرد حکیم را پند ده که زیاده حکیم خواهد شد. مرد عادل را تعلیم ده که علمش خواهد افزود.۹
10 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru; kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.
ابتدای حکمت ترس خداوند است، و معرفت قدوس فطانت می‌باشد.۱۰
11 Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka, ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.
زیرا که به واسطه من روزهای تو کثیر خواهدشد، و سالهای عمر از برایت زیاده خواهدگردید.۱۱
12 Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa; ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.
اگر حکیم هستی، برای خویشتن حکیم هستی. و اگر استهزا نمایی به تنهایی متحمل آن خواهی بود.۱۲
13 Uchitsiru ndi mkazi waphokoso, wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.
زن احمق یاوه‌گو است، جاهل است و هیچ نمی داند،۱۳
14 Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake, pamalo aatali a mu mzinda,
و نزد در خانه خود می‌نشیند، درمکانهای بلند شهر بر کرسی،۱۴
15 kuti aziyitana anthu ongodutsa, amene akunka nayenda njira zawo.
تا راه روندگان رابخواند، و آنانی را که به راههای خود براستی می‌روند.۱۵
16 Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,” ndipo kwa wopanda nzeru amati,
هر‌که جاهل باشد به اینجا برگردد، وبه ناقص العقل می‌گوید:۱۶
17 “Madzi akuba ndiye amatsekemera; chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”
«آبهای دزدیده شده شیرین است، و نان خفیه لذیذ می‌باشد.»۱۷
18 Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko, ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya. (Sheol h7585)
و اونمی داند که مردگان در آنجا هستند، ودعوت‌شدگانش در عمقهای هاویه می‌باشند. (Sheol h7585)۱۸

< Miyambo 9 >