< Miyambo 9 >

1 Nzeru inamanga nyumba yake; inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.
Sapientia aedificavit sibi domum, excidit columnas septem.
2 Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake; inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.
Immolavit victimas suas, miscuit vinum, et proposuit mensam suam.
3 Nzeruyo inatuma adzakazi ake, kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,
Misit ancillas suas ut vocarent ad arcem, et ad moenia civitatis:
4 “Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!” Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,
Siquis est parvulus, veniat ad me. Et insipientibus locuta est:
5 “Bwerani, dzadyeni chakudya changa ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.
Venite, comedite panem meum, et bibite vinum quod miscui vobis.
6 Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo; yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”
Relinquite infantiam, et vivite, et ambulate per vias prudentiae.
7 Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo; aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.
Qui erudit derisorem, ipse iniuriam sibi facit: et qui arguit impium, sibi maculam generat.
8 Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe; dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.
Noli arguere derisorem, ne oderit te. Argue sapientem, et diliget te.
9 Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru; ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.
Da sapienti occasionem, et addetur ei sapientia. Doce iustum, et festinabit accipere.
10 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru; kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.
Principium sapientiae timor Domini: et scientia sanctorum, prudentia.
11 Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka, ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.
Per me enim multiplicabuntur dies tui, et addentur tibi anni vitae.
12 Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa; ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.
Si sapiens fueris, tibimetipsi eris: si autem illusor, solus portabis malum.
13 Uchitsiru ndi mkazi waphokoso, wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.
Mulier stulta et clamosa, plenaque illecebris, et nihil omnino sciens,
14 Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake, pamalo aatali a mu mzinda,
sedit in foribus domus suae super sellam in excelso urbis loco,
15 kuti aziyitana anthu ongodutsa, amene akunka nayenda njira zawo.
ut vocaret transeuntes per viam, et pergentes itinere suo:
16 Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,” ndipo kwa wopanda nzeru amati,
Qui est parvulus, declinet ad me. Et vecordi locuta est:
17 “Madzi akuba ndiye amatsekemera; chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”
Aquae furtivae dulciores sunt, et panis absconditus suavior.
18 Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko, ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya. (Sheol h7585)
Et ignoravit quod ibi sint gigantes, et in profundis inferni convivae eius. (Sheol h7585)

< Miyambo 9 >