< Miyambo 9 >
1 Nzeru inamanga nyumba yake; inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.
La sagesse a bâti sa maison, elle a taillé ses sept colonnes;
2 Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake; inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.
elle a tué ses bêtes, elle a mixtionné son vin, elle a aussi dressé sa table;
3 Nzeruyo inatuma adzakazi ake, kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,
elle a envoyé ses servantes; elle crie sur les sommets des hauteurs de la ville:
4 “Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!” Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,
Qui est simple? qu’il se retire ici. À celui qui est dépourvu de sens, elle dit:
5 “Bwerani, dzadyeni chakudya changa ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.
Venez, mangez de mon pain, et buvez du vin que j’ai mixtionné.
6 Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo; yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”
Laissez la sottise, et vivez, et marchez dans la voie de l’intelligence.
7 Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo; aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.
Qui instruit un moqueur reçoit pour lui-même de la confusion; et qui reprend un méchant [reçoit] pour lui-même une tache.
8 Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe; dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.
Ne reprends pas le moqueur, de peur qu’il ne te haïsse; reprends le sage, et il t’aimera.
9 Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru; ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.
Donne au sage, et il deviendra encore plus sage; enseigne le juste, et il croîtra en science.
10 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru; kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.
La crainte de l’Éternel est le commencement de la sagesse, et la connaissance du Saint est l’intelligence.
11 Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka, ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.
Car par moi tes jours seront multipliés, et des années de vie te seront ajoutées.
12 Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa; ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.
Si tu es sage, tu seras sage pour toi-même; et si tu es moqueur, tu en porteras seul la peine.
13 Uchitsiru ndi mkazi waphokoso, wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.
La femme folle est bruyante, elle est sotte, il n’y a pas de connaissance en elle.
14 Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake, pamalo aatali a mu mzinda,
Et elle s’assied à l’entrée de sa maison sur un trône, dans les lieux élevés de la ville,
15 kuti aziyitana anthu ongodutsa, amene akunka nayenda njira zawo.
pour appeler ceux qui passent sur la route, qui vont droit leur chemin:
16 Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,” ndipo kwa wopanda nzeru amati,
Qui est simple? qu’il se retire ici. Et à celui qui est dépourvu de sens, elle dit:
17 “Madzi akuba ndiye amatsekemera; chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”
Les eaux dérobées sont douces, et le pain [mangé] en secret est agréable!
18 Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko, ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya. (Sheol )
Et il ne sait pas que les trépassés sont là, [et] que ses conviés sont dans les profondeurs du shéol. (Sheol )