< Miyambo 9 >

1 Nzeru inamanga nyumba yake; inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.
Visdommen har bygget sit Hus, har udhugget sine syv Piller;
2 Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake; inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.
hun har slagtet sit Slagtekvæg, blandet sin Vin og dækket sit Bord;
3 Nzeruyo inatuma adzakazi ake, kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,
hun har udsendt sine Piger, hun kalder fra Toppene af Stadens Høje:
4 “Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!” Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,
Hvo der er uvidende, den vende sig hid; og til den, som fattes Forstand, siger hun:
5 “Bwerani, dzadyeni chakudya changa ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.
Kommer hid, æder af mit Brød, og drikker af Vinen, som jeg har blandet.
6 Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo; yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”
Forlader Uvidenhed, saa skulle I leve, og gaar lige frem paa Forstandens Vej.
7 Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo; aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.
Hvo som revser en Spotter, henter sig Spot, og hvo som irettesætter den ugudelige, faar Skændsel til Løn.
8 Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe; dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.
Sæt ikke en Spotter i Rette, at han ikke skal hade dig; sæt en viis i Rette, og han skal elske dig.
9 Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru; ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.
Giv den vise, og han skal blive visere; undervis den retfærdige, og han skal tage til i Lærdom.
10 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru; kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.
Herrens Frygt er Visdoms Begyndelse, og Kundskab om den Hellige er Forstand.
11 Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka, ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.
Thi ved mig skulle dine Dage blive mange, og flere Leveaar skulle vorde dig tillagte.
12 Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa; ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.
Dersom du er viis, er du viis til dit eget Gavn; men spotter du, skal du bære det alene.
13 Uchitsiru ndi mkazi waphokoso, wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.
Daarskaben er en urolig Kvinde, idel Uvidenhed, og kender ikke noget.
14 Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake, pamalo aatali a mu mzinda,
Og hun sidder ved sit Hus's Dør, paa en Stol paa Stadens Høje,
15 kuti aziyitana anthu ongodutsa, amene akunka nayenda njira zawo.
for at kalde paa dem, som gaa forbi ad Vejen, dem, som vandre ret frem paa deres Stier;
16 Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,” ndipo kwa wopanda nzeru amati,
hvo der er uvidende, den vende sig hid; og den, som fattes Forstand, ham taler hun til.
17 “Madzi akuba ndiye amatsekemera; chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”
Stjaalet Vand er sødt, og lønligt Brød er lækkert.
18 Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko, ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya. (Sheol h7585)
Men han ved ikke, at der er Dødninger der; de, som ere indbudne af hende, ere i Dødsrigets Dyb. (Sheol h7585)

< Miyambo 9 >