< Miyambo 8 >

1 Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
Чи ж мудрість не кличе, і не подає свого голосу розум?
2 Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
На верхі́в'ях холмі́в, при дорозі та на перехре́стях стоїть он вона!
3 Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
При брамах, при вході до міста, де вхо́диться в двері, там голосно кличе вона:
4 Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
„До вас, мужі, я кличу, а мій голос до лю́дських синів:
5 Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
Зрозумійте но, не́уки, мудрість, зрозумійте ви розум, безглу́зді!
6 Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
Послухайте, я бо шляхе́тне кажу́, і відкриття́ моїх губ — то просто́та.
7 Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
Бо правду говорять уста́ мої, а лукавство — гидо́та для губ моїх.
8 Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
Всі слова́ моїх уст справедливі, нема в них круті́йства й лука́вства.
9 Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
Усі вони про́сті, хто їх розуміє, і щирі для тих, хто знахо́дить знання́.
10 Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
Візьміть ви карта́ння моє, а не срі́бло, і знання́, добірні́ше від щирого золота:
11 Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
ліпша бо мудрість за пе́рли, і не рівняються їй всі клейно́ди!
12 Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
Я, мудрість, живу разом з розумом, і знахо́джу пізна́ння розва́жне.
13 Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
Страх Господній — лихе все нена́видіти: я нена́виджу пи́ху та гордість, і дорогу лиху та лукаві уста́!
14 Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
В мене рада й огля́дність, я розум, і сила у мене.
15 Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
Мною царю́ють царі, а законода́вці права́ справедливі встано́влюють.
16 Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
Мною пра́влять владики й вельмо́жні, всі праведні су́дді.
17 Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
Я кохаю всіх тих, хто кохає мене, хто ж шукає мене — мене зна́йде!
18 Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
Зо мною багатство та слава, трива́лий маєток та правда:
19 Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
ліпший плід мій від щирого золота й золота чистого, а прибуток мій ліпший за срі́бло добі́рне!
20 Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
Путтю праведною я ходжу́, поміж правних стежо́к,
21 Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
щоб дати багатство в спа́дщину для тих, хто кохає мене, — і я понапо́внюю їхні скарбни́ці!
22 “Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
Господь мене мав на поча́тку Своєї дороги, перше чи́нів Своїх, спервові́ку, —
23 Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
відвіку була я встано́влена, від поча́тку, від праві́ку землі.
24 Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
Наро́джена я, як безо́день іще не було́, коли не було ще джере́л, водою обтя́жених.
25 Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
Наро́джена я, поки го́ри поставлені ще не були́, давніше за па́гірки,
26 lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
коли ще землі не вчинив Він, ні піль, ні початко́вого по́роху все́світу.
27 Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
Коли приправля́в небеса́ — я була́ там, коли кру́га вставля́в на пове́рхні безо́дні,
28 pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
коли хмари умі́цнював Він нагорі́, як джере́ла безо́дні зміцня́в,
29 pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
коли клав Він для моря уста́ва його, щоб його берегі́в вода не перехо́дила, коли ставив осно́ви землі, —
30 Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
то я ма́йстром у Нього була́, і була я весе́лощами день-у-день, радіючи перед обличчям Його кожноча́сно,
31 Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
радіючи на земнім кру́зі Його, а заба́ва моя — із синами людськими!
32 “Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
Тепер же, послухайте, діти, мене, і блаже́нні, хто буде дороги мої стерегти́!
33 Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
Навча́ння послухайте й мудрими станьте, і не відступайте від нього!
34 Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
Блаже́нна люди́на, яка мене слухає, щоб пильнувати при две́рях моїх день-у-день, щоб одві́рки мої берегти́!
35 Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
Хто бо знахо́дить мене, той знахо́дить життя, і оде́ржує милість від Господа.
36 Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”
А хто́ проти мене гріши́ть, ограбо́вує душу свою; всі, хто мене ненави́дить, ті смерть покохали!“

< Miyambo 8 >