< Miyambo 8 >

1 Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
Не виче ли мудрост? И разум не пушта ли глас свој?
2 Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
Наврх висина, на путу, на распутицама стоји,
3 Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
Код врата, на уласку у град, где се отварају врата, виче:
4 Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
Вас вичем, о људи, и глас свој обраћам к синовима људским.
5 Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
Научите се луди мудрости, и безумни оразумите се.
6 Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
Слушајте, јер ћу говорити велике ствари, и усне моје отварајући се казиваће шта је право.
7 Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
Јер уста моја говоре истину, и мрска је уснама мојим безбожност.
8 Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
Праве су све речи уста мојих, ништа нема у њима криво ни изопачено.
9 Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
Све су обичне разумном и праве су онима који налазе знање.
10 Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
Примите наставу моју, а не сребро, и знање радије него најбоље злато.
11 Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
Јер је боља мудрост од драгог камења, и шта је год најмилијих ствари не могу се изједначити с њом.
12 Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
Ја мудрост боравим с разборитошћу, и разумно знање налазим.
13 Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
Страх је Господњи мржња на зло; ја мрзим на поноситост и на охолост и на зли пут и на уста опака.
14 Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
Мој је савет и шта год јесте; ја сам разум и моја је сила.
15 Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
Мном цареви царују, и владаоци постављају правду.
16 Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
Мном владају кнезови и поглавари и све судије земаљске.
17 Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
Ја љубим оне који мене љубе, и који ме добро траже налазе ме.
18 Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
У мене је богатство и слава, постојано добро и правда.
19 Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
Плод је мој бољи од злата и од најбољег злата, и добитак је мој бољи и од најбољег сребра.
20 Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
Путем праведним ходим, посред стаза правице,
21 Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
Да онима који ме љубе дам оно што јесте, и ризнице њихове да напуним.
22 “Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
Господ ме је имао у почетку пута свог, пре дела својих, пре сваког времена.
23 Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
Пре векова постављена сам, пре почетка, пре постања земље.
24 Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
Кад још не беше бездана, родила сам се, кад још не беше извора обилатих водом.
25 Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
Пре него се горе основаше, пре хумова ја сам се родила;
26 lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
Још не беше начинио земље ни поља ни почетка праху васиљенском;
27 Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
Кад је уређивао небеса, онде бејах; кад је размеравао круг над безданом.
28 pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
Кад је утврђивао облаке горе и крепио изворе бездану;
29 pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
Кад је постављао мору међу и водама да не преступају заповести Његове, кад је постављао темеље земљи;
30 Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
Тада бејах код Њега храњеница, бејах Му милина сваки дан, и весељах се пред Њим свагда;
31 Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
Весељах се на васиљени Његовој, и милина ми је са синовима људским.
32 “Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
Тако, дакле, синови, послушајте ме, јер благо онима који се држе путева мојих.
33 Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
Слушајте наставу, и будите мудри, и немојте је одбацити.
34 Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
Благо човеку који ме слуша стражећи на вратима мојим сваки дан и чувајући прагове врата мојих.
35 Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
Јер ко мене налази, налази живот и добија љубав од Господа.
36 Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”
А ко о мене греши, чини криво души својој; сви који мрзе на ме, љубе смрт.

< Miyambo 8 >