< Miyambo 8 >

1 Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
Por acaso a sabedoria não clama, e a inteligência não solta sua voz?
2 Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
Nos lugares mais altos, junto ao caminho, nas encruzilhadas das veredas, ela se põe.
3 Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
Ao lado das portas, à entrada da cidade; na entrada dos portões, ela grita:
4 Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
Varões, eu vos clamo; [dirijo] minha voz aos filhos dos homens.
5 Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
Vós que sois ingênuos, entendei a prudência; e vós que sois loucos, entendei [de] coração.
6 Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
Ouvi, porque falarei coisas nobres; e abro meus lábios para a justiça.
7 Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
Porque minha boca declarará a verdade; e meus lábios abominam a maldade.
8 Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
Todas as coisas que digo com minha boca são justas; não há nelas coisa alguma [que seja] distorcida ou perversa.
9 Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
Todas elas são corretas para aquele que as entende; e justas para os que encontram conhecimento.
10 Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
Aceitai minha correção, e não prata; e o conhecimento mais que o ouro fino escolhido.
11 Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
Porque a sabedoria é melhor do que rubis; e todas as coisas desejáveis nem sequer podem ser comparadas a ela.
12 Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
Eu, a Sabedoria, moro com a Prudência; e tenho o conhecimento do conselho.
13 Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
O temor ao SENHOR é odiar o mal: a soberba e a arrogância, o mal caminho e a boca perversa, eu [os] odeio.
14 Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
A mim pertence o conselho e a verdadeira sabedoria; eu [tenho] prudência e poder.
15 Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
Por meio de mim os reis governam, e os príncipes decretam justiça.
16 Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
Por meio de mim os governantes dominam; e autoridades, todos os juízes justos.
17 Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
Eu amo os que me amam; e os que me buscam intensamente me acharão.
18 Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
Bens e honra estão comigo; [assim como] a riqueza duradoura e a justiça.
19 Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
Meu fruto é melhor que o ouro, melhor que o ouro refinado; e meus produtos melhores que a prata escolhida.
20 Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
Eu faço andar pelo caminho da justiça, no meio das veredas do juízo;
21 Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
Para eu dar herança aos que me amam, e encher seus tesouros.
22 “Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
O SENHOR me adquiriu no princípio de seu caminho; desde antes de suas obras antigas.
23 Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
Desde a eternidade eu fui ungida; desde o princípio; desde antes do surgimento da terra.
24 Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
Quando ainda não havia abismos, eu fui gerada; quando ainda não havia fontes providas de muitas águas.
25 Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
Antes que os montes fossem firmados; antes dos morros, eu fui gerada.
26 lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
Quando ele ainda não tinha feito a terra, nem os campos; nem o princípio da poeira do mundo.
27 Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
Quando preparava os céus, ali eu estava; quando ele desenhava ao redor da face do abismo.
28 pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
Quando firmava as nuvens de cima, quando fortificava as fontes do abismo.
29 pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
Quando colocava ao mar o seu limite, para que as águas não ultrapassassem seu mandado; quando estabelecia os fundamentos da terra.
30 Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
Então eu estava com ele como um pupilo; e eu era seu agrado a cada dia, alegrando perante ele em todo tempo.
31 Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
Alegrando na habitação de sua terra; e [concedendo] meus agrados aos filhos dos homens.
32 “Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
Portanto agora, filhos, ouvi-me; porque bem-aventurados serão [os que] guardarem meus caminhos.
33 Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
Ouvi a correção, e sede sábios; e não a rejeiteis.
34 Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
Bem-aventurado [é] o homem que me ouve; que vigia em minhas portas diariamente, que guarda as ombreiras de minhas entradas.
35 Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
Porque aquele que me encontrar, encontrará a vida; e obterá o favor do SENHOR.
36 Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”
Mas aquele que pecar contra mim fará violência à sua [própria] alma; todos os que me odeiam amam a morte.

< Miyambo 8 >