< Miyambo 8 >

1 Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
Izali mądrość nie woła, i roztropność nie wydaje głosu swego?
2 Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
Na wierzchu wysokich miejsc, przy drodze i na rozstaniu dróg stoi.
3 Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
U bram, kędy się chodzi do miasta, i w wejściu u drzwi woła, mówiąc:
4 Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
Na was wołam, o mężowie! a głos mój obracam do synów ludzkich.
5 Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
Zrozumijcie prostacy ostrożność, a głupi zrozumijcie sercem.
6 Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
Słuchajcie; bo o wielkich rzeczach będę mówił, a otworzenie warg moich opowie szczerość.
7 Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
Zaisteć prawdę mówią usta moje, a niezbożność obrzydliwością jest wargom moim.
8 Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
Sprawiedliwe są wszystkie słowa ust moich; nie masz w nich nic nieprawego ani przewrotnego.
9 Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
Wszystkie są prawe rozumnemu, a uprzejme tym, którzy znajdują umiejętność.
10 Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
Przyjmijcież ćwiczenie moje, a nie srebro, a umiejętność raczej, niż złoto wyborne.
11 Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
Albowiem lepsza jest mądrość niż perły, także wszystkie pożądane rzeczy nie porównają z nią.
12 Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
Ja mądrość mieszkam z roztropnością, i umiejętność ostrożności wynajduję.
13 Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
Bojaźń Pańska jest, mieć w nienawiści złe. Ja nienawidzę pychy, wysokomyślności, i drogi złej, i ust przewrotnych.
14 Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
Przy mnie jest rada, i prawdziwa mądrość; jam jest roztropność, a moc jest moja.
15 Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
Przez mię królowie królują, i książęta stanowią sprawiedliwość.
16 Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
Przez mię książęta panują, i wielmożnymi są wszyscy sędziowie ziemi.
17 Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
Ja miłuję tych, którzy mię miłują; a którzy mię szukają rano, znajdują mię.
18 Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
Bogactwo i sława przy mnie jest; majętność trwała i sprawiedliwość.
19 Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
Lepszy jest owoc mój, niż złoto, i niż najkosztowniejsze złoto, a dochody moje lepsze, niż srebro wyborne.
20 Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
Prowadzę ścieszką sprawiedliwości, pośrodkiem ścieżek sądu,
21 Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
Abym tym, którzy mię miłują, dała w dziedzictwo majętność wieczną, i skarby ich napełniła.
22 “Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
Pan mię miał przy początku drogi swej, przed sprawami swemi, przed wszystkiemi czasy.
23 Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
Przed wieki jestem zrządzona, przed początkiem; pierwej niż była ziemia;
24 Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
Gdy jeszcze nie było przepaści, spłodzonam jest, gdy jeszcze nie było źródeł opływających wodami.
25 Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
Pierwej niż góry założone były, niż były pagórki, spłodzonam jest.
26 lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
Jeszcze był nie uczynił ziemi, i równin, ani początku prochu okręgu ziemskiego.
27 Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
Gdy gotował niebiosa, tamem była; gdy rozmierzał okrągłość nad przepaściami;
28 pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
Gdy utwierdzał obłoki w górze, i umacniał źródła przepaści;
29 pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
Gdy zakładał morzu granice jego, i wodom, aby nie przestępowały rozkazania jego; gdy rozmierzał grunty ziemi:
30 Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
Tedym była u niego jako wychowaniec, i byłam uciechą jego na każdy dzień, grając przed nim na każdy czas.
31 Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
Gram na okręgu ziemi jego, a rozkoszy moje, mieszkać z synami ludzkimi.
32 “Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
Słuchajcież mię tedy teraz, synowie! albowiem błogosławieni, którzy strzegą dróg moich.
33 Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
Słuchajcie ćwiczenia, nabądźcie rozumu, a nie cofajcie się.
34 Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
Błogosławiony człowiek, który mię słucha, czując u wrót moich na każdy dzień, a strzegąc podwoi drzwi moich.
35 Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
Bo kto mię znajduje, znajduje żywot, a otrzymuje łaskę od Pana.
36 Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”
Ale kto grzeszy przeciwko mnie, krzywdę czyni duszy swojej; wszyscy, którzy mię nienawidzą, miłują śmierć.

< Miyambo 8 >