< Miyambo 8 >
1 Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
지혜가 부르지 아니하느냐 명철이 소리를 높이지 아니하느냐
2 Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
그가 길가의 높은 곳과 사거리에 서며
3 Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
성문 곁과 문 어귀와 여러 출입하는 문에서 불러 가로되
4 Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
사람들아 내가 너희를 부르며 내가 인자들에게 소리를 높이노라
5 Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
어리석은 자들아 너희는 명철할지니라 미련한 자들아 너희는 마음이 밝을지니라 너희는 들을지어다
6 Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
내가 가장 선한 것을 말하리라 내 입술을 열어 정직을 내리라
7 Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
내 입은 진리를 말하며 내 입술은 악을 미워하느니라
8 Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
내 입의 말은 다 의로운즉 그 가운데 굽은 것과 패역한 것이 없나니
9 Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
이는 다 총명 있는 자의 밝히 아는 바요 지식 얻은 자의 정직히 여기는 바니라
10 Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
너희가 은을 받지 말고 나의 훈계를 받으며 정금보다 지식을 얻으라
11 Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
대저 지혜는 진주보다 나으므로 무릇 원하는 것을 이에 비교할 수 없음이니라
12 Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
나 지혜는 명철로 주소를 삼으며 지식과 근신을 찾아 얻나니
13 Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
여호와를 경외하는 것은 악을 미워하는 것이라 나는 교만과 거만과 악한 행실과 패역한 입을 미워하느니라
14 Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
내게는 도략과 참 지식이 있으며 나는 명철이라 내게 능력이 있으므로
15 Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
나로 말미암아 왕들이 치리하며 방백들이 공의를 세우며
16 Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
나로 말미암아 재상과 존귀한 자 곧 세상의 모든 재판관들이 다스리느니라
17 Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
나를 사랑하는 자들이 나의 사랑을 입으며 나를 간절히 찾는 자가 나를 만날 것이니라
18 Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
부귀가 내게 있고 장구한 재물과 의도 그러하니라
19 Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
내 열매는 금이나 정금보다 나으며 내 소득은 천은보다 나으니라
20 Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
나는 의로운 길로 행하며 공평한 길 가운데로 다니나니
21 Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
이는 나를 사랑하는 자로 재물을 얻어서 그 곳간에 채우게 하려함이니라
22 “Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
여호와께서 그 조화의 시작 곧 태초에 일하시기 전에 나를 가지셨으며
23 Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
만세 전부터 상고부터, 땅이 생기기 전부터, 내가 세움을 입었나니
24 Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
아직 바다가 생기지 아니하였고 큰 샘들이 있기 전에 내가 이미났으며
25 Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
산이 세우심을 입기 전에 언덕이 생기기 전에 내가 이미 났으니
26 lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
하나님이 아직 땅도 들도 세상 진토의 근원도 짓지 아니하셨을 때에라
27 Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
그가 하늘을 지으시며 궁창으로 해면에 두르실 때에 내가 거기 있었고
28 pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
그가 위로 구름 하늘을 견고하게 하시며 바다의 샘들을 힘 있게하시며
29 pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
바다의 한계를 정하여 물로 명령을 거스리지 못하게 하시며 또 땅의 기초를 정하실 때에
30 Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
내가 그 곁에 있어서 창조자가 되어 날마다 그 기뻐하신 바가 되었으며 항상 그 앞에서 즐거워하였으며
31 Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
사람이 거처할 땅에서 즐거워하며 인자들을 기뻐하였었느니라
32 “Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
아들들아 이제 내게 들으라 내 도를 지키는 자가 복이 있느니라
33 Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
훈계를 들어서 지혜를 얻으라 그것을 버리지 말라
34 Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
누구든지 내게 들으며 날마다 내 문 곁에서 기다리며 문설주 옆에서 기다리는 자는 복이 있나니
35 Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
대저 나를 얻는 자는 생명을 얻고 여호와께 은총을 얻을 것임이니라
36 Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”
그러나 나를 잃는 자는 자기의 영혼을 해하는 자라 무릇 나를 미워하는 자는 사망을 사랑하느니라