< Miyambo 8 >
1 Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
Est-ce que la sagesse ne crie pas, et que la prudence ne fait pas entendre sa voix?
2 Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
Sur les plus hauts et les plus élevés sommets, au-dessus de la voie, se tenant au milieu des sentiers,
3 Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
Près des portes de la cité, à l’entrée même de la ville, elle parle, disant:
4 Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
Ô hommes, c’est à vous que je crie, et ma voix s’adresse aux fils des hommes.
5 Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
Apprenez, ô tout petits, la finesse, et vous, insensés, faites attention.
6 Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
Ecoutez, car je vais parler de grandes choses, et mes lèvres s’ouvriront pour proclamer la droiture.
7 Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
Ma bouche s’exercera à la vérité, et mes lèvres détesteront ce qui est impie.
8 Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
Tous mes discours sont justes, il n’y a rien de dépravé ni de pervers.
9 Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
Ils sont droits pour ceux qui ont de l’intelligence, et équitables pour ceux qui trouvent la science.
10 Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
Recevez ma discipline et non de l’argent: choisissez la doctrine plutôt que l’or.
11 Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
Car mieux vaut la sagesse que toutes les choses les plus précieuses; et tout ce qu’il y a de désirable ne peut lui être comparé.
12 Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
Moi, sagesse, j’habite dans le conseil, et je suis présente aux savantes pensées.
13 Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
La crainte du Seigneur hait le mal: l’arrogance et l’orgueil, une voie dépravée, et une langue double, je les déteste.
14 Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
À moi est le conseil et l’équité: à moi est la prudence, à moi est la force.
15 Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
Par moi les rois règnent, et les législateurs décrètent des choses justes;
16 Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
Par moi les princes commandent, et les puissants rendent la justice.
17 Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
Moi, j’aime ceux qui m’aiment, et ceux qui dès le matin veillent pour me chercher me trouveront.
18 Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
Avec moi sont les richesses et la gloire, des biens superbes, et la justice.
19 Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
Car mieux vaut mon fruit que l’or et les pierres précieuses, et mieux valent mes produits que l’argent le meilleur.
20 Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
Je marche dans les voies de la justice, au milieu des sentiers du jugement,
21 Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
Afin d’enrichir ceux qui m’aiment, et de remplir leurs trésors.
22 “Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
Le Seigneur m’a possédée au commencement de ses voies, avant qu’il fît quelque chose dès le principe.
23 Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
Dès l’éternité j’ai été établie, dès les temps anciens, avant que la terre fût faite.
24 Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
Les abîmes n’étaient pas encore, et moi déjà j’avais été conçue; les sources des eaux n’avaient pas encore jailli:
25 Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
Les montagnes à la pesante masse n’étaient pas encore affermies, et moi, avant les collines, j’étais engendrée:
26 lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
Il n’avait pas encore fait la terre et les fleuves, et les pôles du globe de la terre.
27 Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
Quand il préparait les cieux, j’étais présente: quand par une loi inviolable il entourait d’un cercle les abîmes:
28 pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
Quand il affermissait en haut la voûte éthérée, et qu’il mettait en équilibre les sources des eaux:
29 pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
Quand il mettait autour de la mer ses limites, et qu’il imposait une loi aux eaux, afin qu’elles n’allassent point au-delà de leurs bornes; quand il pesait les fondements de la terre:
30 Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
J’étais avec lui, disposant toutes choses; et je me réjouissais chaque jour, me jouant, en tout temps, devant lui:
31 Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
Me jouant dans le globe de la terre; et mes délices sont d’être avec les fils des hommes.
32 “Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
Maintenant donc, mes fils, écoutez-moi: Bienheureux ceux gardent mes voies.
33 Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
Ecoutez la discipline, et soyez sages, et n’allez pas la rejeter.
34 Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
Bienheureux l’homme qui m’écoute, et qui veille tous les jours à l’entrée de ma demeure, et se tient en observation auprès de ma porte.
35 Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
Celui qui me trouvera trouvera la vie, et puisera le salut dan? le Seigneur:
36 Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”
Mais celui qui péchera contre moi blessera son âme. Tous ceux qui me haïssent aiment la mort.