< Miyambo 8 >

1 Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
La sagesse n'est-elle pas un cri? La compréhension n'élève pas sa voix?
2 Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
Au sommet des hauts lieux, d'ailleurs, là où les chemins se rejoignent, elle se tient debout.
3 Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
Près des portes, à l'entrée de la ville, aux portes d'entrée, elle crie à haute voix:
4 Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
« Je vous appelle, hommes! J'envoie ma voix aux fils de l'humanité.
5 Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
Toi, simple, comprends la prudence! Imbéciles, ayez un cœur compréhensif!
6 Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
Écoutez, car je vais dire des choses excellentes. L'ouverture de mes lèvres est pour les choses justes.
7 Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
Car ma bouche dit la vérité. La méchanceté est une abomination pour mes lèvres.
8 Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
Toutes les paroles de ma bouche sont justes. Il n'y a rien de tordu ou de pervers en eux.
9 Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
Elles sont toutes claires pour celui qui comprend, droit à ceux qui trouvent la connaissance.
10 Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
Recevez mes instructions plutôt que de l'argent, la connaissance plutôt que l'or du choix.
11 Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
Car la sagesse vaut mieux que les rubis. Toutes les choses que l'on peut désirer ne peuvent pas être comparées à elle.
12 Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
« Moi, la sagesse, j'ai fait de la prudence ma demeure. Découvrez la connaissance et la discrétion.
13 Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
La crainte de Yahvé, c'est de haïr le mal. Je déteste l'orgueil, l'arrogance, la mauvaise voie et la bouche perverse.
14 Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
Les conseils et les connaissances solides sont à moi. J'ai la compréhension et le pouvoir.
15 Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
Par moi les rois règnent, et les princes décrètent la justice.
16 Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
C'est par moi que les princes gouvernent, les nobles, et tous les dirigeants justes de la terre.
17 Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
J'aime ceux qui m'aiment. Ceux qui me cherchent assidûment me trouveront.
18 Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
Avec moi, la richesse, l'honneur, la richesse durable et la prospérité.
19 Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
Mon fruit est meilleur que l'or, oui, que l'or fin, mon rendement que l'argent de choix.
20 Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
Je marche dans la voie de la justice, au milieu des chemins de la justice,
21 Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
afin que je puisse donner des richesses à ceux qui m'aiment. Je remplis leurs trésors.
22 “Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
« Yahvé m'a possédé au début de son œuvre, avant ses exploits d'antan.
23 Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
J'ai été établi dès l'éternité, dès le commencement, avant que la terre n'existe.
24 Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
Quand il n'y avait pas de profondeur, je suis né, quand il n'y avait pas de sources abondantes d'eau.
25 Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
Avant que les montagnes ne soient mises en place, avant les collines, je suis né;
26 lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
alors qu'il n'avait pas encore fait la terre et les champs, ni le début de la poussière du monde.
27 Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
Quand il a établi les cieux, j'étais là. Quand il a tracé un cercle à la surface des profondeurs,
28 pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
quand il a établi les nuages au-dessus, quand les sources des profondeurs sont devenues fortes,
29 pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
quand il a donné à la mer sa limite, pour que les eaux ne violent pas son commandement, quand il a tracé les fondations de la terre,
30 Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
alors j'étais l'artisan à ses côtés. J'étais un délice jour après jour, toujours en train de se réjouir devant lui,
31 Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
se réjouissant de tout son monde. Mon plaisir était avec les fils des hommes.
32 “Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
« Maintenant, mes fils, écoutez-moi, car heureux sont ceux qui gardent mes voies.
33 Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
Écoute l'instruction, et sois sage. Ne le refusez pas.
34 Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
Heureux l'homme qui m'écoute, qui veillent quotidiennement à mes portes, qui attendent aux poteaux de ma porte.
35 Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
Car celui qui me trouve trouve la vie, et obtiendra la faveur de Yahvé.
36 Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”
Mais celui qui pèche contre moi fait du tort à sa propre âme. Tous ceux qui me détestent aiment la mort. »

< Miyambo 8 >