< Miyambo 8 >

1 Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
Whether wisdom crieth not ofte; and prudence yyueth his vois?
2 Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
In souereyneste and hiy coppis, aboue the weie, in the myddis of pathis,
3 Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
and it stondith bisidis the yate of the citee, in thilke closyngis, and spekith, and seith, A!
4 Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
ye men, Y crie ofte to you; and my vois is to the sones of men.
5 Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
Litle children, vndirstonde ye wisdom; and ye vnwise men, `perseyue wisdom.
6 Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
Here ye, for Y schal speke of grete thingis; and my lippis schulen be openyd, to preche riytful thingis.
7 Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
My throte schal bithenke treuthe; and my lippis schulen curse a wickid man.
8 Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
My wordis ben iust; no schrewid thing, nether weiward is in tho.
9 Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
`My wordis ben riytful to hem that vndurstonden; and ben euene to hem that fynden kunnyng.
10 Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
Take ye my chastisyng, and not money; chese ye teching more than tresour.
11 Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
For wisdom is betere than alle richessis moost preciouse; and al desirable thing mai not be comparisound therto.
12 Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
Y, wisdom, dwelle in counsel; and Y am among lernyd thouytis.
13 Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
The drede of the Lord hatith yuel; Y curse boost, and pride, and a schrewid weie, and a double tungid mouth.
14 Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
Counseil is myn, and equyte `is myn; prudence is myn, and strengthe `is myn.
15 Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
Kyngis regnen bi me; and the makeris of lawis demen iust thingis bi me.
16 Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
Princis comaunden bi me; and myyti men demen riytfulnesse bi me.
17 Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
I loue hem that louen me; and thei that waken eerli to me, schulen fynde me.
18 Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
With me ben rychessis, and glorie; souereyn richessis, and riytfulnesse.
19 Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
My fruyt is betere than gold, and precyouse stoon; and my seedis ben betere than chosun siluer.
20 Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
Y go in the weies of riytfulnesse, in the myddis of pathis of doom;
21 Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
that Y make riche hem that louen me, and that Y fille her tresouris.
22 “Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
The Lord weldide me in the bigynnyng of hise weies; bifore that he made ony thing, at the bigynnyng.
23 Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
Fro with out bigynnyng Y was ordeined; and fro elde tymes, bifor that the erthe was maad.
24 Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
Depthis of watris weren not yit; and Y was conseyued thanne. The wellis of watris hadden not brokun out yit,
25 Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
and hillis stoden not togidere yit bi sad heuynesse; bifor litil hillis Y was born.
26 lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
Yit he hadde not maad erthe; and floodis, and the herris of the world.
27 Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
Whanne he made redi heuenes, Y was present; whanne he cumpasside the depthis of watris bi certeyn lawe and cumpas.
28 pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
Whanne he made stidfast the eir aboue; and weiede the wellis of watris.
29 pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
Whanne he cumpasside to the see his marke; and settide lawe to watris, that tho schulden not passe her coostis. Whanne he peiside the foundementis of erthe;
30 Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
Y was making alle thingis with him. And Y delitide bi alle daies, and pleiede bifore hym in al tyme,
31 Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
and Y pleiede in the world; and my delices ben to be with the sones of men.
32 “Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
Now therfor, sones, here ye me; blessid ben thei that kepen my weies.
33 Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
Here ye teching, and be ye wise men; and nile ye caste it awei.
34 Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
Blessid is the man that herith me, and that wakith at my yatis al dai; and kepith at the postis of my dore.
35 Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
He that fyndith me, schal fynde lijf; and schal drawe helthe of the Lord.
36 Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”
But he that synneth ayens me, schal hurte his soule; alle that haten me, louen deeth.

< Miyambo 8 >