< Miyambo 8 >
1 Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
Does not wisdom call out, and understanding raise her voice?
2 Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
On the heights overlooking the road, at the crossroads she takes her stand.
3 Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
Beside the gates to the city, at the entrances she cries out:
4 Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
“To you, O men, I call out, and my cry is to the sons of men.
5 Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
O simple ones, learn to be shrewd; O fools, gain understanding.
6 Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
Listen, for I speak of noble things, and the opening of my lips will reveal right.
7 Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
For my mouth will speak the truth, and wickedness is detestable to my lips.
8 Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
All the words of my mouth are righteous; none are crooked or perverse.
9 Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
They are all plain to the discerning, and upright to those who find knowledge.
10 Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
Receive my instruction instead of silver, and knowledge rather than pure gold.
11 Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
For wisdom is more precious than rubies, and nothing you desire compares with her.
12 Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
I, wisdom, dwell together with prudence, and I find knowledge and discretion.
13 Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
To fear the LORD is to hate evil; I hate arrogant pride, evil conduct, and perverse speech.
14 Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
Counsel and sound judgment are mine; I have insight and strength.
15 Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
By me kings reign, and rulers enact just laws;
16 Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
By me princes rule, and all nobles who govern justly.
17 Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
I love those who love me, and those who seek me early shall find me.
18 Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
With me are riches and honor, enduring wealth and righteousness.
19 Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
My fruit is better than gold, pure gold, and my harvest surpasses choice silver.
20 Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
I walk in the way of righteousness, along the paths of justice,
21 Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
bestowing wealth on those who love me and making their treasuries full.
22 “Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
The LORD created me as His first course, before His works of old.
23 Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
From everlasting I was established, from the beginning, before the earth began.
24 Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
When there were no watery depths, I was brought forth, when no springs were overflowing with water.
25 Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
Before the mountains were settled, before the hills, I was brought forth,
26 lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
before He made the land or fields, or any of the dust of the earth.
27 Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
I was there when He established the heavens, when He inscribed a circle on the face of the deep,
28 pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
when He established the clouds above, when the fountains of the deep gushed forth,
29 pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
when He set a boundary for the sea, so that the waters would not surpass His command, when He marked out the foundations of the earth.
30 Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
Then I was a skilled craftsman at His side, and His delight day by day, rejoicing always in His presence.
31 Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
I was rejoicing in His whole world, delighting together in the sons of men.
32 “Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
Now therefore, my sons, listen to me, for blessed are those who keep my ways.
33 Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
Listen to instruction and be wise; do not ignore it.
34 Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
Blessed is the man who listens to me, watching daily at my doors, waiting at the posts of my doorway.
35 Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
For whoever finds me finds life and obtains the favor of the LORD.
36 Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”
But he who fails to find me harms himself; all who hate me love death.”