< Miyambo 8 >

1 Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
Mon ikke Visdommen kalder, løfter Indsigten ikke sin røst?
2 Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
Oppe på Høje ved Vejen, ved Korsveje træder den frem;
3 Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
ved Porte, ved Byens Udgang, ved Dørenes Indgang råber den:
4 Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
Jeg kalder på eder, I Mænd, løfter min Røst til Menneskens Børn.
5 Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
I tankeløse, vind jer dog Klogskab, I Tåber, så få dog Forstand!
6 Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
Hør, thi jeg fører ædel Tale, åbner mine Læber med retvise Ord;
7 Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
ja, Sandhed taler min Gane, gudløse Læber er mig en Gru.
8 Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
Rette er alle Ord af min Mund, intet er falskt eller vrangt;
9 Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
de er alle ligetil for den kloge, retvise for dem der vandt Indsigt
10 Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
Tag ved Lære, tag ikke mod Sølv, tag mod Kundskab fremfor udsøgt Guld;
11 Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
thi Visdom er bedre end Perler, ingen Skatte opvejer den
12 Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
Jeg, Visdom, er Klogskabs Nabo og råder over Kundskab og Kløgt.
13 Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
HERRENs Frygt er Had til det onde. Jeg hader Hovmod og Stolthed, den onde Vej og den falske Mund.
14 Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
Jeg ejer Råd og Visdom, jeg har Forstand, jeg har Styrke.
15 Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
Ved mig kan Konger styre og Styresmænd give retfærdige Love;
16 Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
ved mig kan Fyrster råde og Stormænd dømme Jorden.
17 Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
Jeg elsker dem, der elsker mig, og de, der søger mig, finder mig.
18 Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
Hos mig er der Rigdom og Ære, ældgammelt Gods og Retfærd.
19 Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
Min Frugt er bedre end Guld og Malme, min Afgrøde bedre end kosteligt Sølv.
20 Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
Jeg vandrer på Retfærds Vej. midt hen ad Rettens Stier
21 Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
for at tildele dem, der elsker mig, Gods og fylde deres Forrådshuse.
22 “Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
Mig skabte HERREN først blandt sine Værker, i Urtid, førend han skabte andet;
23 Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
jeg blev frembragt i Evigheden, i Begyndelsen, i Jordens tidligste Tider;
24 Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
jeg fødtes, før Verdensdybet var til, før Kilderne, Vandenes Væld, var til;
25 Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
førend Bjergene sænkedes, før Højene fødtes jeg,
26 lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
førend han skabte Jord og Marker, det første af Jordsmonnets Støv.
27 Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
Da han grundfæsted Himlen, var jeg hos ham, da han satte Hvælv over Verdensdybet.
28 pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
Da han fæstede Skyerne oventil og gav Verdensdybets Kilder deres faste Sted,
29 pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
da han satte Havet en Grænse, at Vandene ej skulde bryde hans Lov, da han lagde Jordens Grundvold,
30 Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
da var jeg Fosterbarn hos ham, hans Glæde Dag efter Dag; for hans Åsyn leged jeg altid,
31 Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
leged på hans vide Jord og havde min Glæde af Menneskens Børn.
32 “Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
Og nu, I Sønner, hør mig! Vel den, der vogter på mine Veje!
33 Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
Hør på Tugt og bliv vise, lad ikke hånt derom!
34 Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
Lykkelig den, der hører på mig, så han daglig våger ved mine Døre og vogter på mine Dørstolper.
35 Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
Thi den, der ftnder mig; finder Liv og opnår Yndest hos HERREN;
36 Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”
men den, som mister mig, skader sig selv; enhver, som hader mig, elsker Døden.

< Miyambo 8 >