< Miyambo 8 >

1 Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
Mon ikke Visdommen raaber, og Forstanden opløfter sin Røst?
2 Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
Paa Toppen af Højene ved Vejen, midt paa Stierne staar den;
3 Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
ved Siden af Portene, ved Udgangen af Staden, ved Indgangen til Portene raaber den:
4 Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
Til eder, I Mænd, vil jeg raabe, og min Røst lyde til Menneskens Børn.
5 Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
I uvidende! fatter Vid; og I Daarer! fatter Forstand.
6 Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
Hører, thi jeg vil tale fyrstelige Ting og aabne mine Læber med Retvished.
7 Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
Thi min Gane taler Sandhed, og Ugudelighed er en Vederstyggelighed for mine Læber.
8 Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
I Retfærdighed ere alle min Munds Ord; der er intet fordrejet eller forvendt i dem.
9 Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
De ere alle rette for den forstandige og ligefremme for dem, som finde Kundskab.
10 Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
Tager imod min Undervisning og ikke imod Sølv og imod Kundskab fremfor udsøgt Guld.
11 Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
Thi Visdom er bedre end Perler, og alle de Ting, man har Lyst til, kunne ikke lignes ved den.
12 Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
Jeg, Visdommen, jeg har taget Bolig i Vidskab og besidder Kundskab om kløgtige Raad.
13 Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
Herrens Frygt er at hade ondt; Hoffærdighed og Hovmodighed og Ondskabs Vej og den Mund, som taler forvendte Ting, hader jeg.
14 Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
Raad og hvad der har Bestand, hører mig til; jeg er Forstand, mig hører Styrke til.
15 Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
Ved mig regere Konger, og ved mig beskikke Fyrster Ret.
16 Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
Ved mig herske Herskere og Høvdinger, alle Dommere paa Jorden.
17 Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
Jeg elsker dem, som elske mig, og de, som søge mig, skulle finde mig.
18 Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
Rigdom og Ære er hos mig, varigt Gods og Retfærdighed.
19 Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
Min Frugt er bedre end Guld og ædelt Malm, og at vinde mig er bedre end udsøgt Sølv.
20 Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
Jeg vandrer paa Retfærdigheds Vej, midt paa Rettens Stier,
21 Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
til at lade dem, som elske mig, arve varigt godt og til at fylde deres Forraadskamre.
22 “Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
Herren ejede mig som sin Vejs Begyndelse, forud for sine Gerninger, fra fordums Tid.
23 Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
Fra Evighed er jeg indsat, fra det første af, før Jorden var.
24 Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
Da Afgrundene endnu ikke vare, er jeg født, da Kilderne, som have meget Vand, ikke vare til.
25 Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
Før Bjergene bleve nedsænkede, før Højene bleve til, er jeg født.
26 lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
Han havde endnu ikke skabt Jorden eller Markerne eller det første af Jordens Støv.
27 Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
Der han beredte Himlene, da var jeg der, der han slog en Kreds oven over Afgrunden;
28 pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
der han befæstede Skyerne heroventil, der Afgrundens Kilder fik deres faste Sted;
29 pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
der han satte Havet dets Grænse, at Vandene ikke skulde overtræde hans Befaling, der han lagde Jordens Grundvold:
30 Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
Da var jeg hos ham som Kunstnerinde, og jeg var hans Lyst Dag for Dag, og jeg legede for hans Ansigt alle Tider;
31 Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
jeg legede i Verden paa hans Jord, og min Lyst var hos Menneskens Børn.
32 “Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
Og nu, Børn, hører mig! og salige ere de, som tage Vare paa mine Veje.
33 Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
Hører Undervisning og bliver vise, og lader den ikke fare!
34 Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
Saligt er det Menneske, som hører mig, saa at han dagligt vaager ved mine Døre og tager Vare paa mine Dørstolper.
35 Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
Thi hvo mig finder, han finder Livet og faar Velbehag hos Herren.
36 Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”
Men hvo, som synder imod mig, skader sin Sjæl; alle, som mig hade, elske Døden.

< Miyambo 8 >