< Miyambo 8 >
1 Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
Cueihnah loh n'khue moenih a? Lungcuei loh a ol a huel dae ta.
2 Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
Longpuei taengkah hmuensang som ah a im kah a hawn ah khaw pai ta.
3 Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
Vangpuei la a kun phai kah vongka hmoi ah khaw thohka kah a rhai ah khaw tamhoe ta.
4 Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
Aw hlang rhoek, nangmih te kang khue tih ka olthang he khaw hlang capa ham ni.
5 Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
Hlangyoe rhoek loh khinglangnah yakming lamtah aka ang rhoek loh lungbuei te yakming lah.
6 Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
Hnatun uh, rhaengsang la ka thui dongah ka hmuilai ka ongnah he vanat la om.
7 Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
Ka ka loh oltak a thuep tih halangnah te ka hmuilai kah a tueilaehkoi ni.
8 Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
Ka ka dongkah duengnah olthui boeih he a hloo vilvak moenih.
9 Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
Aka yakming ham tah boeih langya tih mingnah aka dang ham tah thuem ngawn.
10 Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
Ka thuituennah tangka nen pawt tih, mingnah he sui a coelh lakah khaw lo lah.
11 Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
Cueihnah tah lungvang lakah then tih ngaihnah sarhui khaw te nen te vanat sak thai pawh.
12 Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
Kamah tah cueihnah, khinglangnah neh kho ka sak tih thuepnah dongkah mingnah te ka hmuh.
13 Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
BOEIPA hinyahnah dongah a thae la koevoeinah te thiinah ham ni hoemdamnah neh a thae longpuei khaw, calaak ol khaw ka hmuhuet.
14 Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
Cilsuep neh lungming cueihnah tah kamah taengah, ka yakmingnah neh, kamah ham thayung thamal la om.
15 Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
Kai rhangneh manghai rhoek loh manghai tih boeica rhoek loh duengnah neh a taem uh.
16 Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
Kai rhangneh mangpa rhoek khaw boei uh tih hlangcong boeih loh duengnah lai a tloek uh.
17 Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
Kai aka lung, aka lungnah te ka lungnah tih kai aka toem rhoek loh kai m'hmuh uh.
18 Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
Khuehtawn neh thangpomnah khaw, aka nguel boeirhaeng neh duengnah khaw kamah taengah om.
19 Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
Sui neh suicilh lakah ka thaih then tih ka cangvuei khaw cak lakah cae.
20 Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
Duengnah caehlong ah tiktamnah a hawn khui la ka pongpa.
21 Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
Kai aka lungnah tah ka koe ka pang sak tih a thakvoh te ka koei pah.
22 “Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
Daengrhae daengkhoi lamkah a bibi, hlamat kah a longpuei a tongcuek ah BOEIPA loh kai n'lai coeng.
23 Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
Khosuen lamloh, a lu lamloh, diklai khothoeng lamloh kai n'hloe.
24 Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
Kai ka poe vaengah tuidung khaw ana om pawh, tuisih tui ana phul pawh.
25 Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
Tlang a buek hlan ah som a tueng hlan ah ka cuen coeng.
26 lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
Te vaengah diklai khaw, tollong khaw, lunglai dongkah laipi lamhma khaw ana saii moenih.
27 Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
Vaan a soepsoei ham vaengkah, tuidung hman kah a kueluek te a tarhit ham vaengkah khaw kamah ni.
28 pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
A sang hmuen kah khomong thah sak ham khaw, tuidung tuiphuet tanglue sak ham vaengah khaw,
29 pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
Tuitunli te a rhi suem pah ham vaengah khaw ka om coeng. Te dongah tui loh BOEIPA ol te poe pawh. Diklai kah a yung te a tarhit ham vaengah ka om coeng.
30 Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
Amah taengah bibi thai la ka om tih hnin bal hnin bal hlahmaenah neh ka om. A tue boeih dongah amah mikhmuh ah ka luem.
31 Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
A khohmuen kah lunglai dongah aka luem loh hlang ca te khaw ka hlahmaenah coeng.
32 “Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
Te dongah ca rhoek loh kamah taengah hnatun uh lamtah kamah kah yoethen longpuei ngaithuen uh.
33 Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
Thuituennah he hnatun lamtah cueih lamtah hlahpham boeh.
34 Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
Kamah taengah aka hnatun Ka thohkhaih taengah a hnin a hnin ah aka hak, ka thohka kah rhungsut aka ngaithuen hlang tah a yoethen pai.
35 Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
Kai aka hmu long tah hingnah te a hmuh rhoe a hmuh tih, BOEIPA taengkah kolonah a dang.
36 Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”
Tedae kai aka hmaang long tah a hinglu a huet, kai aka thiinah boeih loh dueknah te a lungnah.