< Miyambo 7 >

1 Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa.
Hijo mío, acepta lo que te digo y saca provecho de mis instrucciones.
2 Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
Haz lo que te digo y vivirás. Observa mis enseñanzas, y estímalas como el objetivo principal de tu vida.
3 Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
Átalas a tus dedos y escríbelas en tu mente.
4 Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
A la sabiduría, dile: “Eres mi hermana”, y considera la inteligencia como tu mejor amiga.
5 Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
Ellas te protegerán de la mujer inmoral, y de la prostituta que viene a ti con palabras seductoras.
6 Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera.
Una vez miré a través de la ventana de mi casa,
7 Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru.
y vi entre los jóvenes inmaduros a uno que era totalmente insensato.
8 Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
Este hombre caminaba por la calle cerca a la esquina de la casa de la prostituta, y tomó el sendero que pasaba por su casa.
9 Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima.
Ya era la hora del crepúsculo, y la luz se desvanecía, mientras llegaba la oscuridad de la noche.
10 Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
Entonces salió esta mujer a su encuentro. Estaba vestida como una prostituta con intenciones engañosas.
11 (Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo.
(Era ruidosa y provocativa, sin deseo de quedarse en casa.
12 Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
Por momentos caminaba por las calles, luego andaba por las plazas, vagabundeando en cada esquina).
13 Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
Lo agarró y lo besó, y con osadía en su rostro, le dijo:
14 “Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
“Ya presenté mi ofrenda de paz hoy, y pagué mis votos.
15 Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
Por eso vine a tu encuentro. ¡Te estaba buscando, y ahora te he encontrado!
16 Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
Mi cama está lista, con sábanas de colores traídas desde Egipto.
17 Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
En mi cama he rociado perfume, aromas de mirra, aloe y canela.
18 Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi!
Ven conmigo, y hagamos el amor hasta el amanecer. ¡Disfrutemos el uno del otro haciendo el amor!
19 Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali:
Mi esposo no está en casa, pues se ha ido a un largo viaje.
20 Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
Se llevó una bolsa de dinero, y no volverá hasta la luna nueva”.
21 Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika.
Así lo convenció con sus palabras, y lo sedujo con su hablar.
22 Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
Él la siguió de inmediato, como buey llevado al matadero. Como ciervo atrapado en una trampa
23 mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
hasta que una lanza traspasa su hígado, como un ave que vuela y queda atrapada, y no sabe que pagará con su vida.
24 Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena.
Así que escúchame ahora, hijo mío, y presta atención a lo que digo.
25 Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake.
No pienses ni siquiera en seguir a tal mujer. No camines por su casa.
26 Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu.
Porque ella ha hecho caer a muchos hombres, y los ha destruido.
27 Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol h7585)
Su casa conduce a la muerte, y en su planta baja se encuentran las moradas de la muerte. (Sheol h7585)

< Miyambo 7 >