< Miyambo 7 >

1 Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa.
Filho meu, guarda as minhas palavras, e esconde dentro de ti os meus mandamentos.
2 Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
Guarda os meus mandamentos, e vive; e a minha lei, como as meninas dos teus olhos.
3 Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
Ata-os aos teus dedos, escreve-os na taboa do teu coração.
4 Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
Dize á sabedoria, Tu és minha irmã; e á prudencia chama parenta.
5 Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
Para te guardarem da mulher alheia, da estrangeira, que lisongeia com as suas palavras.
6 Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera.
Porque da janella da minha casa, por minhas grades olhando eu,
7 Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru.
Vi entre os simplices, descobri entre os moços, um mancebo falto de juizo,
8 Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
Que passava pela rua junto á sua esquina, e seguia o caminho da sua casa;
9 Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima.
No crepusculo, á tarde do dia, na tenebrosa noite e na escuridão;
10 Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
E eis que uma mulher lhe saiu ao encontro, com enfeites de prostituta, e astuta de coração:
11 (Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo.
Esta era alvoroçadora, e contenciosa; não paravam em sua casa os seus pés;
12 Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
Agora por fóra, depois pelas ruas, e espreitando por todos os cantos:
13 Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
E pegou d'elle, e o beijou; esforçou o seu rosto, e disse-lhe:
14 “Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
Sacrificios pacificos tenho comigo; hoje paguei os meus votos.
15 Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
Por isto sahi ao encontro a buscar diligentemente a tua face, e te achei.
16 Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
Já cobri a minha cama com cobertas de tapeçaria, com obras lavradas com linho fino do Egypto.
17 Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
Já perfumei o meu leito com myrrha, aloes, e canella.
18 Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi!
Vem, saciemo-nos de amores até pela manhã: alegremo-nos com amores.
19 Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali:
Porque já o marido não está em sua casa: foi fazer uma jornada ao longe:
20 Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
Um saquitel de dinheiro levou na sua mão: ao dia apontado virá a sua casa.
21 Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika.
Seduziu-o com a multidão das suas palavras, com as lisonjas dos seus labios o persuadiu.
22 Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
Segue-a logo, como boi que vae ao matadouro, e como o louco ao castigo das prisões;
23 mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
Até que a frecha lhe atravesse o figado, como a ave que se apressa para o laço, e não sabe que está armado contra a sua vida.
24 Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena.
Agora pois, filhos, dae-me ouvidos, e estae attentos ás palavras da minha bocca.
25 Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake.
Não se desvie para os seus caminhos o teu coração, e não andes perdido nas suas veredas.
26 Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu.
Porque a muitos feridos derribou; e são muitissimos os que por ella foram mortos.
27 Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol h7585)
Caminhos da sepultura são a sua casa, que descem ás camaras da morte. (Sheol h7585)

< Miyambo 7 >