< Miyambo 7 >
1 Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa.
Mon fils, garde mes paroles; et mes préceptes, mets-les en réserve pour toi. Mon fils,
2 Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
Observe mes commandements et tu vivras; et garde ma loi comme la pupille de ton œil:
3 Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
Lie-la à tes doigts, écris-la sur les tables de ton cœur.
4 Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
Dis à la sagesse: Ma sœur; et la prudence, appelle-la ton amie:
5 Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
Afin qu’elle te préserve d’une femme du dehors, et d’une étrangère, qui rend ses paroles douces.
6 Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera.
Car de la fenêtre de ma maison par les barreaux, j’ai regardé,
7 Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru.
Et je vois les petits enfants, je considère un jeune homme sans cœur,
8 Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
Qui passe dans une rue au coin, et s’avance vers la maison de cette femme,
9 Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima.
À la brume, sur le soir, dans les ténèbres de la nuit et une obscurité profonde.
10 Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
Et voilà qu’au-devant de lui va une femme d’une parure de courtisane, prête à ravir des âmes; causeuse et vagabonde,
11 (Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo.
Inquiète, ne pouvant dans sa maison se tenir sur ses pieds,
12 Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
Tantôt dehors, tantôt dans les places publiques, tantôt aux coins des rues, tendant ses pièges.
13 Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
Et prenant le jeune homme, elle lui donne un baiser, et, d’un visage effronté, elle le flatte, disant:
14 “Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
J’avais voué des victimes pour ton salut; aujourd’hui j’ai acquitté mes vœux;
15 Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
C’est pour cela que je suis sortie au-devant de toi, désirant te voir, et je t’ai rencontré.
16 Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
J’ai entrelacé mon lit de sangles, j’y ai étendu des couvertures brodées d’Egypte;
17 Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
J’ai parfumé ma couche de myrrhe, d’aloës et de cinnamome.
18 Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi!
Viens, enivrons-nous de délices, jouissons de ce que nous avons désiré, jusqu’à ce que le jour paraisse;
19 Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali:
Mon mari n’est pas à sa maison: il est parti pour un voyage très long;
20 Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
Il a pris avec lui le sac où est l’argent; c’est à la pleine lune qu’il doit revenir à sa maison.
21 Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika.
Elle l’a enlacé par la multitude de ses paroles; et par les flatteries de ses lèvres, elle l’a entraîné.
22 Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
Aussitôt, il la suit comme un bœuf conduit pour servir de victime, et comme un agneau bondissant et ignorant, l’insensé, qu’on l’entraîne pour le lier,
23 mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
Jusqu’à ce qu’une flèche ait percé son foie; comme un oiseau va précipitamment dans un filet, ignorant qu’il s’agit du danger de son âme.
24 Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena.
Maintenant donc, mon fils, écoute-moi, et sois attentif aux paroles de ma bouche.
25 Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake.
Que ton esprit ne soit point entraîné dans les voies de cette femme; ne t’égare pas dans ses sentiers;
26 Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu.
Car elle a renversé beaucoup de blessés qu’elle avait faits, et les plus forts, quels qu’ils fussent, ont été tués par elle.
27 Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol )
Ce sont des voies de l’enfer que sa maison; voies pénétrant jusque dans les profondeurs de la mort. (Sheol )