< Miyambo 7 >

1 Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa.
Mon fils, garde mes paroles et conserve au-dedans de toi mes commandements.
2 Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
Observe mes commandements, et tu vivras; garde mon enseignement comme la prunelle de tes yeux;
3 Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
Lie-les à tes doigts, écris-les sur la table de ton cœur.
4 Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
Dis à la sagesse: Tu es ma sœur; et appelle la prudence ton amie;
5 Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
Afin qu'elles te préservent de la femme étrangère, et de la femme d'autrui, qui se sert de paroles flatteuses.
6 Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera.
Comme je regardais par la fenêtre de ma maison, à travers mes treillis,
7 Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru.
Je remarquai parmi les insensés, et je considérai parmi les jeunes gens, un jeune homme dépourvu de sens,
8 Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
Qui passait par la rue, au coin où se tenait une de ces femmes, et qui suivait le chemin de sa maison,
9 Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima.
Sur le soir, à la fin du jour, lorsque la nuit devenait noire et obscure.
10 Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
Et voici, une femme vint au-devant de lui, parée en courtisane, et pleine de ruse.
11 (Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo.
Elle était bruyante et sans retenue, et ses pieds ne demeuraient point dans sa maison;
12 Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
Tantôt dans les rues, tantôt dans les places, elle épiait à chaque coin.
13 Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
Elle le prit, et l'embrassa, et d'un visage effronté lui dit:
14 “Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
Je devais un sacrifice de prospérité; aujourd'hui j'ai acquitté mes vœux.
15 Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
C'est pourquoi je suis sortie au-devant de toi, pour te chercher avec empressement, et je t'ai trouvé.
16 Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
J'ai orné mon lit de tapis, d'étoffes aux couleurs diverses, en fil d'Égypte.
17 Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
J'ai parfumé ma couche de myrrhe, d'aloès et de cinnamome.
18 Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi!
Viens, enivrons-nous de délices jusqu'au matin, réjouissons-nous dans les plaisirs.
19 Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali:
Car mon mari n'est pas à la maison; il est allé bien loin en voyage;
20 Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
Il a pris avec lui un sac d'argent; il ne retournera en sa maison qu'à la nouvelle lune.
21 Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika.
Elle l'entraîna à force de paroles, et le fit tomber par la flatterie de ses lèvres.
22 Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
Il s'en alla aussitôt après elle, comme un bœuf s'en va à la boucherie, et comme un fou qu'on lie pour être châtié,
23 mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
Jusques à ce qu'une flèche lui perce le foie; comme un oiseau qui se précipite vers le lacet, ne sachant pas qu'il est tendu contre sa vie.
24 Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena.
Maintenant donc, mes enfants, écoutez-moi, et soyez attentifs aux paroles de ma bouche.
25 Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake.
Que ton cœur ne se détourne point vers les voies de cette femme, et qu'elle ne te fasse point égarer dans ses sentiers.
26 Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu.
Car elle en a fait tomber plusieurs, blessés à mort, et grand est le nombre de ceux qu'elle a tués.
27 Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol h7585)
Sa maison est le chemin du Sépulcre; il descend aux demeures de la mort. (Sheol h7585)

< Miyambo 7 >