< Miyambo 7 >
1 Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa.
Mi sone, kepe thou my wordis; and kepe myn heestis to thee. Sone, onoure thou the Lord, and thou schalt be `myyti; but outakun hym drede thou not an alien.
2 Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
Kepe thou myn heestis, and thou schalt lyue; and my lawe as the appil of thin iyen.
3 Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
Bynde thou it in thi fyngris; write thou it in the tablis of thin herte.
4 Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
Seie thou to wisdom, Thou art my sistir; and clepe thou prudence thi frendesse.
5 Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
That it kepe thee fro a straunge womman; and fro an alien womman, that makith hir wordis swete.
6 Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera.
For whi fro the wyndow of myn hous bi the latijs Y bihelde; and Y se litle children.
7 Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru.
I biholde a yong man coward,
8 Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
that passith bi the stretis, bisidis the corner; and he
9 Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima.
goith niy the weie of hir hous in derk tyme, whanne the dai drawith to niyt, in the derknessis and myst of the nyyt.
10 Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
And lo! a womman, maad redi with ournement of an hoore to disseyue soulis, meetith hym, and sche is a ianglere, and goynge about,
11 (Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo.
and vnpacient of reste, and mai not stonde in the hous with hir feet;
12 Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
and now without forth, now in stretis, now bisidis corneris sche `aspieth.
13 Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
And sche takith, and kissith the yong man; and flaterith with wowynge cheer, and seith, Y ouyte sacrifices for heelthe;
14 “Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
to dai Y haue yolde my vowis.
15 Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
Therfor Y yede out in to thi meetyng, and Y desiride to se thee; and Y haue founde thee.
16 Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
Y haue maad my bed with coordis, Y haue arayed with tapetis peyntid of Egipt;
17 Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
Y haue bispreynt my bed with myrre, and aloes, and canel.
18 Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi!
Come thou, be we fillid with tetis, and vse we collyngis that ben coueitid; til the dai bigynne to be cleer.
19 Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali:
For myn hosebonde is not in his hows; he is goon a ful long weie.
20 Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
He took with hym a bagge of money; he schal turne ayen in to his hous in the dai of ful moone.
21 Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika.
Sche boonde hym with many wordis; and sche drow forth hym with flateryngis of lippis.
22 Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
Anoon he as an oxe led to slayn sacrifice sueth hir, and as a ioli lomb and vnkunnynge; and the fool woot not, that he is drawun to bondys,
23 mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
til an arowe perse his mawe. As if a brid hastith to the snare; and woot not, that it is don of the perel of his lijf.
24 Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena.
Now therfor, my sone, here thou me; and perseyue the wordis of my mouth.
25 Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake.
Lest thi soule be drawun awei in the weies of hir; nether be thou disseyued in the pathis of hir.
26 Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu.
For sche castide doun many woundid men; and alle strongeste men weren slayn of hir.
27 Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol )
The weies of helle is hir hous; and persen in to ynnere thingis of deeth. (Sheol )