< Miyambo 7 >

1 Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa.
My son, keep my words, and lay up my commandments with thee.
2 Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
Keep my commandments, and live; and my law as the apple of thy eye.
3 Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
Bind them upon thy fingers, write them upon the table of thy heart.
4 Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
Say to wisdom, Thou art my sister; and call understanding thy kinswoman:
5 Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
That they may keep thee from the adulteress, from the stranger which flattereth with her words.
6 Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera.
For at the window of my house I looked through my casement,
7 Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru.
And beheld among the simple ones, I discerned among the youths, a young man void of understanding,
8 Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
Passing through the street near her corner; and he went the way to her house,
9 Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima.
In the twilight, in the evening, in the black and dark night:
10 Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
And, behold, there met him a woman with the attire of an harlot, and subtil of heart.
11 (Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo.
(She is loud and stubborn; her feet abide not in her house:
12 Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
Now is she outside, now in the streets, and lieth in wait at every corner.)
13 Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
So she caught him, and kissed him, and with an impudent face said to him,
14 “Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
I have peace offerings with me; this day have I paid my vows.
15 Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
Therefore I came forth to meet thee, diligently to seek thy face, and I have found thee.
16 Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
I have decked my bed with coverings of tapestry, with carved works, with fine linen of Egypt.
17 Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
I have perfumed my bed with myrrh, aloes, and cinnamon.
18 Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi!
Come, let us take our fill of love until the morning: let us solace ourselves with loves.
19 Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali:
For my husband is not at home, he is gone a long journey:
20 Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
He hath taken a bag of money with him, and will come home at the day appointed.
21 Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika.
With her much fair speech she caused him to yield, with the flattering of her lips she seduced him.
22 Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
He goeth after her quickly, as an ox goeth to the slaughter, or as a fool to the correction of the stocks;
23 mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
Till an arrow striketh through his liver; as a bird hasteth to the snare, and knoweth not that it is for his life.
24 Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena.
Now therefore hearken to me, O ye children, and attend to the words of my mouth.
25 Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake.
Let not thy heart decline to her ways, go not astray in her paths.
26 Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu.
For she hath cast down many wounded: yea, many strong men have been slain by her.
27 Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol h7585)
Her house is the way to hell, going down to the chambers of death. (Sheol h7585)

< Miyambo 7 >