< Miyambo 7 >
1 Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa.
My son, keep my words and store up my commands within yourself.
2 Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
Keep my commands and live and keep my instruction as the apple of your eye.
3 Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
Tie them on your fingers; write them on the tablet of your heart.
4 Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
Say to wisdom, “You are my sister,” and call understanding your kinsman,
5 Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
in order to keep yourself from the adulterous woman, from the immoral woman with her smooth words.
6 Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera.
At the window of my house I was looking out through the lattice.
7 Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru.
I looked at the naive people, and I noticed among the young men a youth who had no sense.
8 Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
That young man passed down the street near her corner, and he went toward her house.
9 Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima.
It was twilight, in the evening of the day, at the time of night and darkness.
10 Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
There a woman met him, dressed like a prostitute, with a false heart.
11 (Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo.
She was loud and wayward; her feet did not stay at home.
12 Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
Now in the streets, then in the market place, and at every corner she waited in ambush.
13 Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
So she grabbed him and kissed him, with a strong face she said to him,
14 “Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
“I made my peace offering today, I paid my vows,
15 Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
so came I out to meet you, to eagerly seek your face, and I have found you.
16 Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
I have spread coverings on my bed, colored linens from Egypt.
17 Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
I have sprinkled my bed with myrrh, aloes, and cinnamon.
18 Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi!
Come, let us drink our fill of love until morning; let us take great pleasure in acts of love.
19 Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali:
For my husband is not at his house; he has gone on a long journey.
20 Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
He took a bag of money with him; he will return on the day of the full moon.”
21 Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika.
With much talk she turned him; with her smooth lips she misled him.
22 Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
He went after her suddenly like an ox going to slaughter, like a deer caught in a trap,
23 mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
until an arrow pierces through its liver. He was like a bird rushing into a snare. He did not know that it would cost his life.
24 Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena.
Now, my sons, listen to me; pay attention to the words of my mouth.
25 Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake.
May your heart not turn aside onto her paths; do not be led astray onto her paths.
26 Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu.
She has caused many people to fall down pierced; her dead victims are very many.
27 Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol )
Her house is on the paths to Sheol; they go down to the dark bedrooms of death. (Sheol )