< Miyambo 7 >

1 Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa.
My son, keep my words, and lay up my precepts with thee. Son,
2 Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
Keep my commandments, and thou shalt live: and my law as the apple of thy eye:
3 Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
Bind it upon thy fingers, write it upon the tables of thy heart.
4 Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
Say to wisdom: Thou art my sister: and call prudence thy friend,
5 Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
That she may keep thee from the woman that is not thine, and from the stranger who sweeteneth her words.
6 Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera.
For I look out of the window of my house through the lattice,
7 Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru.
And I see little ones, I behold a foolish young man,
8 Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
Who passeth through the street by the corner, and goeth nigh the way of her house.
9 Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima.
In the dark, when it grows late, in the darkness and obscurity of the night,
10 Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
And behold a woman meeteth him in harlot’s attire prepared to deceive souls; talkative and wandering,
11 (Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo.
Not bearing to be quiet, not able to abide still at home,
12 Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
Now abroad, now in the streets, now lying in wait near the corners.
13 Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
And catching the young man, she kisseth him, and with an impudent face, flattereth, saying:
14 “Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
I vowed victims for prosperity, this day I have paid my vows.
15 Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
Therefore I am come out to meet thee, desirous to see thee, and I have found thee.
16 Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
I have woven my bed with cords, I have covered it with painted tapestry, brought from Egypt.
17 Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
I have perfumed my bed with myrrh, aloes, and cinnamon.
18 Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi!
Come, let us be inebriated with the breasts, and let us enjoy the desired embraces, till the day appear.
19 Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali:
For my husband is not at home, he is gone a very long journey.
20 Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
He took with him a bag of money: he mill return home the day of the full moon.
21 Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika.
She entangled him with many words, and drew him away with the flattery of her lips.
22 Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
Immediately he followeth her as an ox led to be a victim, and as a lamb playing the wanton, and not knowing that he is drawn like a fool to bonds,
23 mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
Till the arrow pierce his liver: as if a bird should make haste to the snare, and knoweth not that his life is in danger.
24 Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena.
Now therefore, my son, hear me, and attend to the words of my mouth.
25 Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake.
Let not thy mind be drawn away in her ways: neither be thou deceived with her paths.
26 Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu.
For she hath cast down many wounded, and the strongest have been slain by her.
27 Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol h7585)
Her house is the way to hell, reaching even to the inner chambers of death. (Sheol h7585)

< Miyambo 7 >