< Miyambo 7 >
1 Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa.
Min Søn, vogt dig mine Ord, mine bud må du gemme hos dig;
2 Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
vogt mine bud, så skal du leve, som din Øjesten vogte du, hvad jeg har lært dig;
3 Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
bind dem om dine Fingre, skriv dem på dit Hjertes Tavle,
4 Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
sig til Visdommen: "Du er min Søster!" og kald Forstanden Veninde,
5 Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
at den må vogte dig for Andenmands Hustru, en fremmed Kvinde med sleske Ord.
6 Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera.
Thi fra mit Vindue skued jeg ud, jeg kigged igennem mit Gitter;
7 Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru.
og blandt de tankeløse så jeg en Yngling, en uden Vid blev jeg var blandt de unge;
8 Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
han gik på Gaden tæt ved et Hjørne, skred frem på Vej til hendes Hus
9 Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima.
i Skumringen henimod Aften, da Nat og Mørke brød frem.
10 Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
Og se, da møder Kvinden ham i Skøgedragt, underfundig i Hjertet;
11 (Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo.
løssluppen, ustyrlig er hun, hjemme fandt hendes Fødder ej Ro;
12 Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
snart på Gader, snart på Torve, ved hvert et Hjørne lurer hun; -
13 Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
hun griber i ham og kysser ham og siger med frække Miner;
14 “Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
"Jeg er et Takoffer skyldig og indfrier mit Løfte i Dag,
15 Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
gik derfor ud for at møde dig, søge dig, og nu har jeg fundet dig!
16 Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
Jeg har redt mit Leje med Tæpper, med broget ægyptisk Lærred
17 Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
jeg har stænket min Seng med Myrra, med Aloe og med Kanelbark;
18 Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi!
kom, lad os svælge til Daggry i Vellyst, beruse os i Elskovs Lyst!
19 Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali:
Thi Manden er ikke hjemme, - på Langfærd er han draget;
20 Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
Pengepungen tog han med, ved Fuldmåne kommer han hjem!"
21 Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika.
Hun lokked ham med mange fagre Ord, forførte ham med sleske Læber;
22 Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
tankeløst følger han hende som en Tyr, der føres til Slagtning, som en Hjort, der løber i Nettet,
23 mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
til en Pil gennemborer dens Lever, som en Fugl, der falder i Snaren, uden at vide, det gælder dens Liv.
24 Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena.
Hør mig da nu, min Søn, og lyt til min Munds Ord!
25 Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake.
Ej bøje du Hjertet til hendes Veje, far ikke vild på hendes Stier;
26 Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu.
thi mange ligger slagne, hvem hun har fældet, og stor er Hoben, som hun slog ihjel.
27 Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol )
Hendes Hus er Dødsrigets Veje, som fører til Dødens Kamre. (Sheol )