< Miyambo 6 >

1 Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole, ngati walonjeza kumulipirira mlendo,
Me ba, sɛ woadi akagyinamu ama ɔyɔnko bi, sɛ wode wo biribi asi awowa ama obi,
2 ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena, wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako.
sɛ nea wokae ayi ka ama wo na sɛ wʼano asɛm afiri ayi wo a,
3 Tsono popeza iwe mwana wanga wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse: pita msanga ukamupemphe mnansi wako; kuti akumasule!
ɛno de yɛ eyi, me ba, na fa tetew wo ho, sɛ ɔyɔnko nsa aka wo no nti: fa ahobrɛase kɔ nʼanim; na kɔ so pa wo yɔnko no kyɛw!
4 Usagone tulo, usawodzere.
Mma wʼani nkum na ntɔ nko.
5 Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje, ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka.
Gye wo ho, sɛnea ɔforote guan fi ɔbɔmmɔfo nsam anaa sɛnea anomaa guan fi ofirisumfo afiri mu no.
6 Pita kwa nyerere, mlesi iwe; kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!
Ɔkwadwofo, kɔ ɔtɛtea nkyɛn; hwɛ nʼakwan, na hu nyansa!
7 Zilibe mfumu, zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,
Onni ɔsahene, onni ɔhwɛfo anaa sodifo bi,
8 komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.
nanso ɔde aduan sie wɔ ahuhurubere mu, ɔboaboa nnuan ano wɔ twabere.
9 Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe? Kodi tulo tako tidzatha liti?
Wo, ɔkwadwofo, wobɛda akosi da bɛn? Wubenyan bere bɛn?
10 Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,
Nna kakra, nkotɔ kakra, nsa a woabobɔw de rehome kakra,
11 umphawi udzakugwira ngati mbala ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.
ɛbɛma ohia aba wo so sɛ ɔkwanmukafo na ahokyere atow akyere wo sɛnea okura otuo.
12 Munthu wachabechabe, munthu woyipa, amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa,
Onipa teta ne ohuhuni a odi atoro kyin,
13 amatsinzinira maso ake, namakwakwaza mapazi ake ndi kulozaloza ndi zala zake,
nea obu nʼani, na ɔde ne nan yɛ nsɛnkyerɛnne na ɔde ne nsateaa kyerɛkyerɛ ade,
14 amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu.
nea ɔde ne koma mu nnaadaa bɔ pɔw bɔne, na ɔde mpaapaemu ba bere biara.
15 Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa; adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa.
Ɛno nti amanehunu bɛba no so prɛko pɛ; wɔbɛsɛe no mpofirim, a wɔrenya ano aduru.
16 Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo, zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:
Nneɛma asia na Awurade mpɛ, nneɛma ason na ɛyɛ nʼakyiwade:
17 maso onyada, pakamwa pabodza, manja akupha munthu wosalakwa,
ani a ɛtra ntɔn, atoro tɛkrɛma, nsa a ɛka mogya a edi bem gu,
18 mtima wokonzekera kuchita zoyipa, mapazi othamangira msanga ku zoyipa,
koma a edwen amumɔyɛ ho, anan a etutu mmirika kɔyɛ bɔne,
19 mboni yonama yoyankhula mabodza komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.
ɔdansekurumni a odi atoro ne onipa a ɔde mpaapaemu ba anuanom mu.
20 Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako; ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako.
Me ba, tie wʼagya ahyɛde na nnyaa wo na nkyerɛkyerɛ mu.
21 Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse, uzimangirire mʼkhosi mwako.
Fa kyekyere wo koma ho daa; na fa kyekyere wɔ kɔn mu.
22 Ukamayenda, zidzakulozera njira; ukugona, zidzakulondera; ukudzuka, zidzakuyankhula.
Wonantew a, ɛbɛkyerɛ wo kwan; sɛ woda a, ɛbɛwɛn wo; sɛ wunyan a, ɛbɛkasa akyerɛ wo.
23 Paja malamulo awa ali ngati nyale, malangizowa ali ngati kuwunika, ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo moyo weniweni,
Na saa ahyɛde yi yɛ kanea saa nkyerɛkyerɛ yi yɛ hann, na ahohyɛso nteɛso yi yɛ nkwa kwan,
24 kukupulumutsa kwa mkazi wadama, zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere.
ɛtwe wo fi ɔbea a onni suban pa no ho, fi ɔbeawarefo huhuni tɛkrɛmadɛ ho.
25 Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake, asakukope ndi zikope zake,
Mma wo kɔn nnɔ nʼahoɔfɛ, mma nʼani akyideda no ntwetwe wo,
26 paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse.
efisɛ oguamanfo ma wʼanuonyam yɛ sɛ brodosin, na obi yere gyigye wo kɔ owu mu.
27 Kodi munthu angathe kutenga moto zovala zake osapsa?
Obi betumi asɔ gya agu ne srɛ so a nhyew nʼatade ana?
28 Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto mapazi ake osapserera?
Obi betumi anantew nnyansramma so a mpumpunnya mmobɔ nʼanan ho ana?
29 Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina. Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa.
Saa na ɔbarima a ɔne ɔbarima foforo yere da no te; obiara a ɔde ne nsa bɛka no no, remfa ne ho nni da.
30 Paja anthu sayinyoza mbala ikaba chifukwa chakuti ili ndi njala.
Nnipa mmu ɔkorɔmfo a wakowia ade animtiaa sɛ ɔkɔm de no na ɔde rekodwudwo ano nti.
31 Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri, ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake.
Mmom, sɛ wɔkyere no a, ɛsɛ sɛ otua mmɔho ason; sɛ ɛbɛma wahwere ne fi agyapade nyinaa mpo a.
32 Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru. Wochita zimenezi amangodziwononga yekha.
Ɔbarima a ɔsɛe aware no nni adwene; obiara a ɔyɛ saa no sɛe ne ho.
33 Adzalandira mabala ndi mʼnyozo, ndipo manyazi ake sadzamuchokera.
Ɔhwe ne animguase na obenya, na nʼahohora rempepa da.
34 Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa, ndipo sadzachita chifundo pobwezera.
Ninkutwe hwanyan okunu abufuw na sɛ ɔtɔ were a, ahummɔbɔ biara nni mu.
35 Iye savomera dipo lililonse; sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.
Ɔrennye mpata biara; na ɔbɛpo adanmude, sɛ ɛso sɛ dɛn mpo a.

< Miyambo 6 >