< Miyambo 6 >

1 Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole, ngati walonjeza kumulipirira mlendo,
Mwanangu, kama utaweka pesa zako kuwa dhamana kwa mkopo wa jirani yako; kama ukitoa ahadi yako katika mkopo wa mtu usiyemjua,
2 ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena, wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako.
basi umejiwekea mtego mwenyewe na umenaswa kwa maneno ya kinywa chako.
3 Tsono popeza iwe mwana wanga wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse: pita msanga ukamupemphe mnansi wako; kuti akumasule!
Mwanagu, ukinaswa kwa maneno yako mwenyewe, fanya haya ili kujiokoa, kwa kuwa umeangukia kwenye mikono ya jirani yako; nenda unyenyekee na ufanye shauri mbele ya jirani yako.
4 Usagone tulo, usawodzere.
Usiruhusu usingizi katika macho yako wala kope za macho yako kusinzia.
5 Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje, ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka.
Jiokoe mwenyewe kama swala kutoka katika mkono wa mwindaji, kama ndege kutoka katika mkono wa mwinda ndege.
6 Pita kwa nyerere, mlesi iwe; kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!
Wewe mtu mvivu, mwangalie mchwa, zitafakari njia zake ili kupata busara.
7 Zilibe mfumu, zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,
Hana akida, afisa au mtawala,
8 komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.
lakini huandaa chakula chake wakati wa joto na wakati wa mavuno huweka hazina ili kula baadaye.
9 Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe? Kodi tulo tako tidzatha liti?
Ewe mtu mvivu, utalala hata lini? Wakati gani utainuka usingizini?”
10 Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,
Lala kidogo, sizia kidogo, kunja mikono kupumzika kidogo” -
11 umphawi udzakugwira ngati mbala ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.
ndipo umasikini wako utakapokujia kama mporaji na uhitaji wako kama askari wa vita.
12 Munthu wachabechabe, munthu woyipa, amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa,
Mtu asiyefaa-mtu mwovu- huishi kwa kauli za udanganyifu wake,
13 amatsinzinira maso ake, namakwakwaza mapazi ake ndi kulozaloza ndi zala zake,
akipepesa macho yake, akiashilia kwa miguu yake na kusonta kwa videle vyake.
14 amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu.
Hufanya njama za uovu kwa hila ya moyo wake; daima huchochea faraka.
15 Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa; adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa.
Kwa hiyo msiba wake utamkumba kwa ghafula, punde atavunjika vibaya wala hatapona.
16 Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo, zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:
Kuna vitu sita ambavyo Yehova huvichukia, saba ambavyo ni chukizo kwake.
17 maso onyada, pakamwa pabodza, manja akupha munthu wosalakwa,
Macho ya mtu mwenye kiburi, ulimi wa uongo, mikono inayomwaga damu ya watu maasumu,
18 mtima wokonzekera kuchita zoyipa, mapazi othamangira msanga ku zoyipa,
moyo unaobuni njama mbaya, miguu inayokimbilia maovu upesi,
19 mboni yonama yoyankhula mabodza komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.
shahidi asemaye uongo na apandaye faraka kati ya ndugu.
20 Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako; ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako.
Mwanangu, itii amri ya baba yako na wala usiyaache mafundisho ya mama yako.
21 Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse, uzimangirire mʼkhosi mwako.
Uyafunge katika moyo wako siku zote; yafunge kwenye shingo yako.
22 Ukamayenda, zidzakulozera njira; ukugona, zidzakulondera; ukudzuka, zidzakuyankhula.
utembeapo, yatakuongoza; ulalapo yatakulinda, na uamkapo yatakufundisha.
23 Paja malamulo awa ali ngati nyale, malangizowa ali ngati kuwunika, ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo moyo weniweni,
Maana amri ni taa, na mafundisho ni nuru; kinga za kuadilisha za njia ya uzima.
24 kukupulumutsa kwa mkazi wadama, zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere.
Yanakulinda dhidi ya mwanamke malaya, dhidi ya maneno laini ya uzinzi.
25 Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake, asakukope ndi zikope zake,
Moyoni mwako usiutamani uzuri wake wala usitekwe katika kope zake.
26 paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse.
Kulala na malaya inaweza kugharimu bei ya kipande cha mkate, lakini mke wa mtu mwingine inagharimu uzima wako wote.
27 Kodi munthu angathe kutenga moto zovala zake osapsa?
Je mtu anaweza kubeba moto katika kifua chake bila kuuguza mavazi yake?
28 Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto mapazi ake osapserera?
Je mtu anaweza kutembea juu ya makaa bila kuchomwa miguu yake?
29 Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina. Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa.
Ndivyo alivyo mtu alalaye na mke wa jirani yake; yule alalaye na huyo mke hatakosa adhabu.
30 Paja anthu sayinyoza mbala ikaba chifukwa chakuti ili ndi njala.
Watu hawawezi kumdharau mwizi kama anaiba ili kukidhi hitaji lake la njaa.
31 Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri, ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake.
Walakini akimatwa, atalipa mara saba ya kile alichoiba; lazima atoe kila kitu cha thamani katika nyumba yake.
32 Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru. Wochita zimenezi amangodziwononga yekha.
Mtu anayefanya uzinzi hana akili; hufanya hiyo kwa uharibifu wake mwenyewe.
33 Adzalandira mabala ndi mʼnyozo, ndipo manyazi ake sadzamuchokera.
Anasitahili aibu na majeraha na fedheha yake haiwezi kuondolewa.
34 Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa, ndipo sadzachita chifundo pobwezera.
Maana vivu humghadhibisha mtu; hatakuwa na huruma wakati wa kulipa kisasi chake.
35 Iye savomera dipo lililonse; sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.
Ujapompa zawadi nyingi, hatakubali mbadala wa kusuruhishwa wala kulipwa.

< Miyambo 6 >