< Miyambo 6 >

1 Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole, ngati walonjeza kumulipirira mlendo,
Fili mi, si spoponderis pro amico tuo, defixisti apud extraneum manum tuam,
2 ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena, wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako.
illaqueatus es verbis oris tui, et captus propriis sermonibus.
3 Tsono popeza iwe mwana wanga wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse: pita msanga ukamupemphe mnansi wako; kuti akumasule!
Fac ergo quod dico fili mi, et temetipsum libera: quia incidisti in manum proximi tui. Discurre, festina, suscita amicum tuum:
4 Usagone tulo, usawodzere.
ne dederis somnum oculis tuis, nec dormitent palpebrae tuae.
5 Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje, ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka.
Eruere quasi damula de manu, et quasi avis de manu aucupis.
6 Pita kwa nyerere, mlesi iwe; kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!
Vade ad formicam o piger, et considera vias eius, et disce sapientiam:
7 Zilibe mfumu, zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,
quae cum non habeat ducem, nec praeceptorem, nec principem,
8 komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.
parat in aestate cibum sibi, et congregat in messe quod comedat.
9 Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe? Kodi tulo tako tidzatha liti?
Usquequo piger dormies? quando consurges e somno tuo?
10 Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,
Paululum dormies, paululum dormitabis, paululum conseres manus ut dormias:
11 umphawi udzakugwira ngati mbala ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.
et veniet tibi quasi viator, egestas, et pauperies quasi vir armatus. Si vero impiger fueris, veniet ut fons messis tua, et egestas longe fugiet a te.
12 Munthu wachabechabe, munthu woyipa, amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa,
Homo apostata, vir inutilis, graditur ore perverso,
13 amatsinzinira maso ake, namakwakwaza mapazi ake ndi kulozaloza ndi zala zake,
annuit oculis, terit pede, digito loquitur,
14 amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu.
pravo corde machinatur malum, et omni tempore iurgia seminat.
15 Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa; adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa.
huic extemplo veniet perditio sua, et subito conteretur, nec habebit ultra medicinam.
16 Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo, zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:
Sex sunt, quae odit Dominus, et septimum detestatur anima eius:
17 maso onyada, pakamwa pabodza, manja akupha munthu wosalakwa,
Oculos sublimes, linguam mendacem, manus effundentes innoxium sanguinem,
18 mtima wokonzekera kuchita zoyipa, mapazi othamangira msanga ku zoyipa,
cor machinans cogitationes pessimas, pedes veloces ad currendum in malum,
19 mboni yonama yoyankhula mabodza komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.
proferentem mendacia testem fallacem, et eum, qui seminat inter fratres discordias.
20 Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako; ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako.
Conserva fili mi praecepta patris tui, et ne dimittas legem matris tuae.
21 Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse, uzimangirire mʼkhosi mwako.
Liga ea in corde tuo iugiter, et circumda gutturi tuo.
22 Ukamayenda, zidzakulozera njira; ukugona, zidzakulondera; ukudzuka, zidzakuyankhula.
Cum ambulaveris, gradiantur tecum: cum dormieris, custodiant te, et evigilans loquere cum eis.
23 Paja malamulo awa ali ngati nyale, malangizowa ali ngati kuwunika, ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo moyo weniweni,
quia mandatum lucerna est, et lex lux, et via vitae increpatio disciplinae:
24 kukupulumutsa kwa mkazi wadama, zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere.
ut custodiant te a muliere mala, et a blanda lingua extraneae.
25 Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake, asakukope ndi zikope zake,
Non concupiscat pulchritudinem eius cor tuum, nec capiaris nutibus illius:
26 paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse.
pretium enim scorti vix est unius panis: mulier autem viri pretiosam animam capit.
27 Kodi munthu angathe kutenga moto zovala zake osapsa?
Numquid potest homo abscondere ignem in sinu suo, ut vestimenta illius non ardeant?
28 Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto mapazi ake osapserera?
aut ambulare super prunas, ut non comburantur plantae eius?
29 Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina. Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa.
sic qui ingreditur ad mulierem proximi sui, non erit mundus cum tetigerit eam.
30 Paja anthu sayinyoza mbala ikaba chifukwa chakuti ili ndi njala.
Non grandis est culpa, cum quis furatus fuerit: ut esurientem impleat animam:
31 Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri, ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake.
deprehensus tamen reddet septuplum, et omnem substantiam domus suae tradet.
32 Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru. Wochita zimenezi amangodziwononga yekha.
Qui autem adulter est, propter cordis inopiam perdet animam suam:
33 Adzalandira mabala ndi mʼnyozo, ndipo manyazi ake sadzamuchokera.
turpitudinem et ignominiam congregat sibi, et opprobrium illius non delebitur.
34 Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa, ndipo sadzachita chifundo pobwezera.
quia zelus et furor viri non parcet in die vindictae,
35 Iye savomera dipo lililonse; sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.
nec acquiescet cuiusquam precibus, nec suscipiet pro redemptione dona plurima.

< Miyambo 6 >